Malifalensi a Utumiki komasoti moyo wasu wa chikhilisitu Kabuku kamisonkhano
JANUARY 11-17
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | LEVITIKO 20-21
“Yehova epatula ŵanthu ŵake kumitundu iyakine”
it-1-CN pedji 1199
Cholowa
Cholowa ndi katundu kapena zinthu zina zimene mwiniwake akamwalira zimaperekedwa kwa woyenera kupatsidwa zinthuzo, kaya mwana wake kapena kwa munthu wina. Mawu a Chiheberi amene anawamasulira kuti “cholowa” ndi na·chalahʹ. Mawuwa amanena za kulandira kapena kupereka zinthu zakumtundu kwa munthu wina, ndipo nthawi zambiri wolandirayo amalowa m’malo mwa womwalirayo. (Nu 26:55; Eze 46:18) Mawu ena ofanana nawo akuti ya·rashʹ nthawi zina ankagwiritsidwa ntchito ponena za “wolowa m’malo” koma nthawi zambiri ankagwiritsidwa ntchito ponena za “kutenga katundu.” (Ge 15:3; Le 20:24) Mawuwa amatanthauzanso ‘kuthamangitsa anthu pamalo n’kulanda malowo,’ mwankhondo. (De 2:12; 31:3) Mawu a Chigiriki amene anawagwiritsa ntchito ponena za cholowa ndi wofanana ndi mawu akuti kleʹros. Poyamba mawuwa ankatanthauza “maere” koma kenako anayamba kutanthauza “kukhala ndi gawo” ndipo kenako anayamba kutanthauza “cholowa.”—Mt 27:35; Mac 1:17; 26:18.
it-1 pedji 317 ndim. 2
Tunyoni
Pavuli pakuti chigumula chachitika, Nowa epeleka “nyama zituŵa zundalala” pamozi na nyama, ziyakine monga nsembe. (Ge 8:18-20) Kupita kwa nthawe Mulungu eyamba kuvomeja kuti ŵanthu akokulya tunyoni kupatulapo milopa yake. (Ge 9:1-4; yelekezelani na Le 7:26; 17:13.) Nkhalidwe ‘ituŵa’ ya tunyoni tuyakine twa panthawe yamene iyo yenzeziŵika na chizindikilo chiyakine cha Mulungu chamene chenzechitisha kuti atuvomeleje kunkhala nsembe: mawu ayakine a m’Baibolo owonesha kuti monga mwamene chakulya mwachukatishiliwa ntchito paliye kanyoni kenzewonewa kunkhala “kodesewa” mpaka pechinkhazikishiwa chilamulo cha Mose. (Le 11:13-19, 46, 47; 20:25; De 14:11-20) M’Baibolo muliye malamulo amene ofotokoza bwino-bwino kuti ni tunyoni totyani twamene twenzeziŵika kuti “n’todesewa”. Tetyo chifukwa chakuti chiŵelengelo chikulu cha tunyoni twamene utu todesewa twenzenkhala tunyoni tupaya nyama olo payakine kulya nyama yakufwa kale ni tunyonilini tonse twamene twenzewonewa kunkhala todesewa. (Onani pa HOOPOE.) Lamulo yolesha kulya mitundu iyakine ya nyama olo tunyoni ichosewa pavuli pakuti pangano inyowani yankhazikishiwa, molingana na mwechiujiliwa Petulo na Mulungu mmasomphenya ŵake.—Mac 10:9-15.
Kusakila-sakila Mfundo zingatiyavye
it-1 pedji 563
Kulicheka
Chilamulo cha Mulungu chenzelesha mwapadela kuti osalicheka-cheka muŵili chifukwa cha munthu wafwa. (Le 19:28; 21:5; De 14:1) Chilamulo chenzelesha kuchita vamene ivi chifukwa chakuti Isiraeli wenze ntundu utuŵa kwa Yehova, ndipo wenze chuma chake chapadela. (De 14:2) Kuyangijila pamene apo, Isiraeli enzefunika kupewa kulambila mafano kwa ntundu uliwonse. Tetyo enzefunikalini kuchita nawo miyambo iyakine yenzechita ŵanthu amitundu iyakine monga kulicheka-cheka akafwelewa. Ivi venze teti chifukwa chakuti Aisiraeli enzeziŵa vuchitika munthu akamwalila komasoti enze na chikhulupilo chakuti akufwa azauke. (Da 12:13; Ahe 11:19) Kuyangijila pamene apo kulesha Aisiraeli kuti osati akoliwononga kwiŵayavya kuti akolemekeza muŵili wawo wamene ni chilengedwe cha Mulungu.
JANUARY 18-24
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | LEVITIKO 22-23
“Nthawe ya vikondwelelo ili na tanthauzo kuli sewo”
it-1-CN pedji 826-827
Chikondwerero cha Mikate Yopanda Chofufumitsa
Tsiku loyamba la Chikondwerero cha Mikate Yopanda Chofufumitsa linkakhala la msonkhano wapadera komanso tsiku la sabata. Pa tsiku lachiwiri, pa Nisani 16, Aisiraeli ankafunika kupititsa kwa wansembe mtolo umodzi wa balere woyamba kucha ku Palesitina. Chikondwererochi chisanachitike, sankayenera kudya mbewu zimene akolola kumene, kuzigwiritsa ntchito popangira mkate kapena kudya zokazinga. Wansembe ankapereka kwa Yehova mophiphiritsa zokolola zoyamba kuchazi mochita kuweyula mtolo wake uku ndi uku. Mwana wa nkhosa wopanda chilema, wosapitirira chaka chimodzi ankaperekedwanso monga nsembe yopsereza limodzi ndi nsembe ya ufa wothira mafuta komanso vinyo wa nsembe yachakumwa. (Le 23:6-14) Panalibe lamulo loti aziwotcha mbewu kapena ufa wake paguwa, ngati zimene pambuyo pake ansembe anayamba kuchita. Sikuti pachikondwererochi Aisiraeli ankangopereka nsembe ya zokolola zoyamba kucha monga gulu basi, koma banja kapena munthu aliyense yemwe akufuna kuthokoza Mulungu chifukwa cha zinthu zomwe anali nazo, ankathanso kupereka nsembe yoyamikira.—Eks 23:19; De 26:1, 2.
Kufunika kwa Mwambowu. Kudya mikate yopanda chofufumitsa kunali kogwirizana ndi malangizo amene Yehova anapatsa Mose omwe amapezeka pa Ekisodo 12:14-20. Ena mwa malangizowo chinali chiletso champhamvu chomwe chili muvesi 19 chakuti: “Musamadzapezeke mtanda wa ufa wokanda wokhala ndi chofufumitsa m’nyumba zanu kwa masiku 7.” Pa Deuteronomo 16:3, mikate yopanda chofufumitsa imatchedwa “mkate wa nsautso,” ndipo chaka chilichonse mikateyi inkakumbutsa Ayuda kuti anachoka ku Iguputo mofulumira kwambiri (analibe nthawi yoika zofufumitsa m’mikate yawo [Eks 12:34]). Zimenezi zinkakumbutsanso Aisiraeli kuti Yehova anawapulumutsa ku ukapolo komanso masautso awo, monga mmene Yehova ananenera kuti, “uzichita zimenezi kuti uzikumbukira tsiku limene unatuluka m’dziko la Iguputo, masiku onse a moyo wako.” Ufulu umene anali nawo pa nthawiyo monga mtundu komanso kuzindikira kuti Yehova ndi amene anawapulumutsa, zinali zifukwa zomveka zomwe zinawachititsa kuti apange chikondwerero chawo choyamba pa zikondwerero zikuluzikulu zitatu zimene ankachita chaka chilichonse.—De 16:16.
it-2-CN pedji 598 ndim. 2
Pentekosite
Zimene ankachita ndi tirigu woyamba kucha, zinali zosiyana ndi zimene ankachita ndi balere woyamba kucha. Ankatenga ufa wa tirigu wokwana magawo awiri mwa magawo 10 a muyezo wa efa (omwe ndi malita 4.4), kuikamo zofufumitsa n’kupanga mikate iwiri. Mikateyi inkafunika kuchokera ‘m’nyumba mwawo’ kutanthauza kuti inkafunika kukhala yofanana ndi imene ankapanga tsiku ndi tsiku monga chakudya chapakhomo, osati yongopangira zochitika zapadera. (Le 23:17) Mikate imeneyi ankaipereka nsembe pamodzi ndi nsembe yopsereza komanso nsembe yamachimo. Ankaperekanso ana a nkhosa amphongo awiri monga nsembe yachiyanjano. Wansembe ankaweyula mikateyo ndi ana a nkhosawo pamaso pa Yehova. Poweyulapo ankanyamula mikateyo komanso nthuli za nyamayo ndipo ankayendetsa manja ake uku ndi uku posonyeza kuti akupereka zinthuzo kwa Yehova. Akamaliza, zinthuzo zinkakhala zake ndipo ankazidya monga nsembe yachiyanjano.—Le 23:18-20.
JANUARY 25-31
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | LEVITIKO 24-25
“Chaka cha ufulu komasoti kumasuliwa kwasu”
it-1 pedji 871
Ufulu
Mulungu opeleka ufulu. Yehova ni Mulungu wamene opeleka ufulu. Yove epulumusa ntundu wa Isiraeli ku ukapolo ku Iguputo. Ndipo eŵauja kuti, keno akomvwila malamulo ŵake, azankhalelini osauka. (De 15:4, 5) Davide elaŵila za ‘kunkhala uliye nkhaŵa iliyonse’ musanja zaku Yelusalemu. (Sl 122:6, 7) Tetyo Chilamulo, chenzenena kuti, keno munthu wasauka, enzefunika kuligulisa kuti ankhale kapolo na cholinga chakuti akolipezela vofunika pamoyo wake komasoti kupezela vinthu vofunika banja yake. Koma, Chilamulo chenzenenasoti kuti Munthu wamene uyu enzenkhala na ufulu mu chaka cha 7 pa ukapolo wake. (Eks 21:2) Mu chaka chaufulu (chamene chenzechitika pa vyaka 50 vilivonse) ufulu wenzelengezewa kuli ŵanthu onse onkhala m’chalo chamene icho. Kapolo aliyense Wachihebeli enzemasuliwa, ndipo enzejokela ku malo ŵake amene enze mphaso olo kuti cholowa chake.—Le 25:10-19.
it-1-CN pedji 1200 ndim. 2
Cholowa
Popeza malo ankakhala chuma chakubanja ndipo ankachoka kwa m’badwo wina kupita m’badwo wina, sizikanatheka kuti akagulitsidwa azikhala a munthu wogulayo mpaka kalekale. Malo ankagulitsidwa potengera kuchuluka kwa zokolola zomwe wogulayo adzapeze pamalowo ndipo mtengo wake unkadalira zaka zimene zatsala kuti Chaka cha Ufulu chifike. Chakachi chikafika malo onse amene anagulitsidwa ankabwezedwa kwa eniake ngati eniakewo sanathe kuwagulanso kapena kuwawombola. (Le 25:13, 15, 23, 24) Lamuloli linkagwiranso ntchito pa nyumba zomwe zinali m’mizinda yopanda mipanda, chifukwa nazonso zinkatengedwa ngati malo. Koma nyumba ikakhala kuti inali mumzinda wa mpanda, mwayi wogulanso nyumbayo unkakhalapo kwa chaka chimodzi ndipo ngati mwiniwake sanathe kuigulanso pa nthawi imeneyi, inkakhala ya wogulayo. Pomwe nyumba zomwe zinali m’mizinda ya Alevi, mwayi wozigulanso unkakhalapo mpaka kalekale chifukwa Alevi analibe cholowa cha malo.—Le 25:29-34.
FEBRUARY 1-7
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | LEVITIKO 26-27
“Mwatingalondelele madaliso a Yehova”
it-1-CN pedji 223 ndim. 3
Kuopa
Chifukwa cha mmene Yehova ankagwiritsira ntchito Mose komanso kuchitira naye zinthu, Moseyo ankachita zinthu zamphamvu pamaso pa Aisiraeli. (De 34:10, 12; Eks 19:9) Anthu amene anali ndi chikhulupiriro ankamuopa chifukwa cha udindo waukulu umene anali nawo. Iwo ankadziwa kuti Mulungu ankalankhula nawo kudzera mwa iye. Aisiraeli ankafunikanso kuopa malo opatulika a Yehova. (Le 19:30; 26:2) Zimenezi zikutanthauza kuti ankafunika kumalemekeza kwambiri malo opatulika, kulambira Yehova m’njira imene amavomereza komanso kutsatira malamulo ake onse.
w91 1/3 pedji 17 ndim. 10
Lolani kuti “ntendele wa Mulungu” ukoteteza ntima wanu
10 Yehova euja ntundu wamene uyo kuti: “Mukapitilija kukonkheja malangizo ŵangu na kusunga malamulo ŵangu, nizakulokwesheleni mvula panthawe yake, chalo chizakupaseni chakulya komasoti vimiti va mminda vizakupaseni vitwazi vake. Komasoti nizakupaseni ntendele m’chalo chamene icho, mwakuti muzayone pansi, paliye okuyofyani; M’chalo chanu muzapezekelini vinyama voyofya vakusanga, ndipo m’chalo chanu muzapitelini lupanga. Tetyo nizapite pakati panu komasoti nizakuwonesheni kuti newo nine Mulungu wanu, ndipo mwewo muzankhale ŵanthu ŵangu.” (Levitiko 26:3, 4, 6, 12) Aisiraeli sembe ekwanisha kunkhala mwantendele komasoti osangalala chifukwa chakuti ove enze otetezeka kwa adani ŵawo, enze na chuma chinyinji chakuthupi, komasoti enze paushamwali wotang’a na Yehova. Koma vamene ivi venzedalila pa kukonkheja kwawo Chilamulo cha Mulungu.—Salimo 119:165.
Kusakila-sakila Mfundo zingatiyavye
it-2-CN pedji 617
Miliri
Yobwera Chifukwa Chosiya Kutsatira Chilamulo cha Mulungu. Aisiraeli anachenjezedwa kuti akadzasiya kutsatira pangano lawo ndi Mulungu, Mulunguyo ‘adzawatumizira mliri.’ (Le 26:14-16, 23-25; De 28:15, 21, 22) Malemba amasonyeza kuti kukhala ndi thanzi labwino, kaya mwakuthupi kapena mwauzimu, ndi kogwirizana ndi madalitso a Yehova (De 7:12, 15; Sl 103:1-3; Miy 3:1, 2, 7, 8; 4:21, 22; Chv 21:1-4), pamene matenda ndi ogwirizana ndi uchimo komanso kupanda ungwiro. (Eks 15:26; De 28:58-61; Yes 53:4, 5; Mt 9:2-6, 12; Yoh 5:14) Ngakhale kuti nthawi zina Yehova ankachititsa kuti munthu adwale matenda enaake nthawi yomweyo, ngati mmene zinaliri ndi khate la Miriamu, Uziya komanso Gehazi (Nu 12:10; 2Mb 26: 16-21; 2Mf 5:25-27), zikuoneka kuti nthawi zambiri matenda kapena miliri zinkakhala zotsatira za zolakwa zimene anthu kapena mtundu wachita. Ankakhala kuti akukolola zimene anafesa. Ankakumana ndi mavuto chifukwa cha zochita zawo zoipa. (Aga 6:7, 8) Ponena za anthu achiwerewere, mtumwi Paulo ananena kuti Mulungu “anawasiya kuti achite zonyansa, kuti matupi awo achitidwe chipongwe . . . ndi kulandiriratu mphoto yoyenerera kulakwa kwawo.”—Aro 1:24-27.
FEBRUARY 8-14
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | NUMERI 1-2
“Yehova olinganija gulu yake mwadongosolo”
w94 1/12 pedji 9 ndim. 4
Malo oyenelela olambilila Yehova pa moyo wasu
4 Yelekezelani kuti muli m’lulu ndipo mulolesha malo ŵenzenkhala Aisiraeli m’chipululu, kansi sembe muwona chinji? Malo akulu koma adongosolo ya mahema mwanzenkhala ŵanthu pafupifupi 3 miliyoni olo kupitilila, eunganijiwa m’magulu a mafuko atatu kumpoto, kumwela, ku mmawa, komasoti ku nchingulo. Posonjelela pafupi, sembe muwonasoti gulu iyakine pafupi na pakati pa misasa. M’tumagulu 4 twamene utu twa mahema mwenzenkhala mabanja a fuko ya Levi. Pakati ngapo-ngapo penze “chitenti cha misonkhano” olo kuti chihema chamene chenzechingilijiwe na nyula chamene Aisiraeli a “aluso” chechipanga molingana na malangizo a Yehova.—Numeri 1:52, 53; 2:3, 10, 17, 18, 25; Ekisodo 35:10.
it-1-CN pedji 397 ndim. 4
Msasa
Msasa wa Aisiraeliwu unkakhala waukulu kwambiri. Munkakhala asilikali okwana 603,550, akazi ndi ana, anthu achikulire, olumala, Alevi 22,000 komanso ‘khamu la anthu a mitundu ina yosiyanasiyana,’ ndipo n’kutheka kuti onse pamodzi ankakwana 3 miliyoni kapena kuposa. (Eks 12: 38, 44; Nu 3:21-34, 39) Sizikudziwika kuti msasa umenewu unkakwana malo aakulu bwanji chifukwa anthu amanena zosiyanasiyana. Baibulo limati Aisiraeli atamanga msasa moyang’anizana ndi Yeriko m’Zigwa za Mowabu, msasawo ‘unayambira ku Beti-yesimoti mpaka ku Abele-sitimu.’—Nu 33:49.
Kusakila-sakila Mfundo zingatiyavye
it-2-CN pedji 764
Kulembetsa M’kaundula
Nthawi zambiri ankalemba dzina la munthu ndiponso mzere wobadwira potengera fuko lake komanso banja lomwe anabadwira. Cholinga sichinali kungopeza chiwerengero cha anthu. Kulembetsa m’kaundula komwe kumatchulidwa m’Baibulo kunkachitika pa zifukwa zosiyanasiyana monga zokhudza kukhoma msonkho, kupeza oyenera kupita kunkhondo kapenanso kusankha okagwira ntchito pamalo opatulika (ngati anthuwo ndi Alevi).
FEBRUARY 15-21
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | NUMERI 3-4
“Ntchito ya Alevi”
it-2-CN pedji 683 ndim. 3
Wansembe
M’Pangano la Chilamulo. Pamene Aisiraeli anali akapolo ku Iguputo, Yehova anadzipatulira mwana aliyense woyamba kubadwa pakati pawo, pa nthawi imene anapha mwana aliyense woyamba kubadwa m’dziko la Iguputo ndi mliri wa 10. (Eks 12:29; Nu 3:13) Ana oyamba kubadwa amenewa anakhala a Yehova kuti azimuchitira utumiki wapadera. Yehova akanatha kusankha ana onse aamuna oyamba kubadwa a Aisiraeli kuti azikhala ansembe komanso kuti azisamalira malo opatulika. Koma m’malomwake, anaona kuti n’koyenera kungotenga amuna achilevi kuti azichita utumiki umenewu. Pachifukwa chimenechi, Yehova analola kuti amuna achilevi alowe m’malo mwa amuna oyamba kubadwa a mafuko ena 12 (Efuraimu ndi Manase omwe anali ana a Yosefe ankatengedwa monga mafuko awiri). Atawerenga ana onse aamuna oyamba kubadwa a mwezi umodzi kupita m’tsogolo, panapezeka kuti ana omwe si achilevi anachuluka ndi 273 kuposa ana oyamba kubadwa achilevi. Chifukwa cha zimenezi, Yehova analamula Mose kuti atenge masekeli asanu (omwe ndi madola 11) pa munthu aliyense monga dipo la ana aamuna oyamba kubadwa a Isiraeli okwana 273 omwe anapitirira chiwerengero cha Alevi, ndipo ndalamazo akazipereke kwa Aroni ndi ana ake. (Nu 3:11-16, 40-51) Zimenezi zisanachitike, Yehova anali atapatula kale amuna a m’banja la Aroni omwe anali a fuko la Levi kuti azitumikira monga ansembe mu Isiraeli.—Nu 1:1; 3:6-10.
it-2-CN pedji 241
Alevi
Ntchito Zawo. Fuko la Alevi linkapangidwa ndi mabanja atatu a ana a Levi, omwe anali Gerisoni (Gerisomu), Kohati ndi Merari. (Ge 46:11; 1Mb 6:1, 16) Banja lililonse linkapatsidwa malo pafupi ndi chihema m’chipululu. Banja la Kohati, lomwe munali Aroni, linkakhala kutsogolo kwa chihema kum’mawa, pomwe Akohati ena onse ankakhala kum’mwera kwa chihema. Agerisoni ankakhala kumadzulo ndipo Amerari ankakhala kumpoto. (Nu 3:23, 29, 35, 38) Ntchito yomanga, kuphwasula komanso kunyamula chihema inali ya Alevi. Nthawi yosamuka ikakwana, Aroni ndi ana ake ankatsitsa nsalu imene inkalekanitsa Malo Oyera ndi Malo Oyera Koposa ndipo ankaphimbira likasa la chipangano, maguwa a nsembe ndi zinthu zina zopatulika. Akohati ndi amene ankanyamula zinthuzi. Agerisoni ankanyamula nsalu za chihema, nsalu zophimbira, nsalu zotchinga pakhomo, nsalu za mpanda wa bwalo ndiponso zingwe za chinsalu (zimenezi ziyenera kuti zinali zingwe za chihema chenichenicho). Pomwe Amerari anali ndi ntchito yosamalira mafelemu, mizati, zitsulo zokhazikapo nsanamira, zikhomo ndi zingwe zolimbitsira nsanamira (izi zinali zingwe za nsanamira za bwalo la chihema).—Nu 1:50, 51; 3:25, 26, 30, 31, 36, 37; 4:4-33; 7:5-9.
it-2-CN pedji 241
Alevi
M’nthawi ya Mose, Mlevi ankayamba kugwira ntchito zake zonse akakwanitsa zaka 30 ndipo ntchito zake zinali monga kunyamula chihema komanso zinthu zogwiritsa ntchito pachihemachi akamasamuka. (Nu 4:46-49) Alevi ankayamba kugwira ntchito zina akakwanitsa zaka 25 koma sizinkakhala zolemetsa ngati kunyamula chihema. (Nu 8:24) Munthawi ya Mfumu Davide, zakazi zinachepetsedwa kufika pa 20. Davide ananena kuti anachita zimenezi chifukwa choti pa nthawiyi chihema sichinkafunikanso kunyamulidwa chifukwa chinali choti chilowedwa m’malo ndi kachisi. Alevi ankasiya kugwira ntchito zawo akakwanitsa zaka 50. (Nu 8:25, 26; 1Mb 23:24-26) Alevi ankafunika azidziwa kwambiri Chilamulo chifukwa ankayenera kuwerengera anthu pagulu komanso kuphunzitsa Chilamulocho.—1Mb 15:27; 2Mb 5:12; 17:7-9; Ne 8:7-9.
FEBRUARY 22-28
CHUMA CHUPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | NUMERI 5-6
“Kansi mwewo mungaŵakonkheje tyani Anaziri?”
it-2-CN pedji 477
Mnaziri
Panali malamulo atatu akuluakulu amene munthu amene walumbira kukhala Mnaziri ankayenera kuwatsatira: (1) Sankafunika kumwa chakumwa chilichonse choledzeretsa. Sankafunikanso kudya kapena kumwa chilichonse chochokera ku mtengo wa mpesa. Mwachitsanzo, sankafunika kudya mphesa zosapsa, zakupsa kapena zouma. Sankafunikanso kumwa madzi a mphesa zongothyola kumene, zosasa kapena viniga wochokera ku mphesazo. (2) Sankafunika kumeta tsitsi la m’mutu mwawo. (3) Sankafunikanso kugwira mtembo wa munthu, kaya munthuyo akhale bambo awo, mayi awo, mchimwene wawo kapena mchemwali wawo.—Nu 6:1-7.
Malumbiro Apadera. Munthu amene wachita lonjezo lapadera limeneli ankayenera kukhala “Mnaziri [kutanthauza wodzipereka] kwa Yehova.” Sankafunika kumakokomeza moyo wodzimana umene ankakhala n’cholinga chofuna kudzionetsera kwa anthu. M’malomwake ‘iye ankakhala woyera kwa Yehova masiku onse a unaziri wake.’—Nu 6:2, 8.
Choncho zinthu zimene Anaziri ankafunira kumachita, zinali ndi tanthauzo lapadera pa nkhani ya kulambira Yehova. Mofanana ndi mkulu wansembe, amene sankafunika kugwira mtembo wa munthu chifukwa cha udindo wake, ngakhale munthuyo atakhala wachibale wake wapafupi, nayenso Mnaziri sankafunika kuchita zimenezi. Komanso mkulu wansembe ndiponso ansembe ena, chifukwa cha udindo wawo wapadera, sankafunika kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa akamachita utumiki wawo wopatulika pamaso pa Yehova.—Le 10:8-11; 21:10, 11.
Komanso Mnaziri (m’Chiheberi na·zirʹ) ankayenera kukhala “woyera mwa kusiya tsitsi lake la kumutu kuti likule,” ndipo zimenezi zinkachititsa kuti anthu azimuzindikira mosavuta kuti ndi Mnaziri. (Nu 6:5) Mawu a Chiheberi omwewa akuti na·zirʹ ankagwiritsidwanso ntchito ponena za mitengo ya mphesa ‘yosadulira’ pa nthawi ya Sabata lopatulika komanso Chaka cha Ufulu. (Le 25:5, 11) Chochititsanso chidwi n’chakuti kachitsulo kamene kankakhala patsogolo panduwira ya mkulu wansembe, pomwe pankagobedwa mawu akuti “Chiyero n’cha Yehova,” ankakatchula kuti “chizindikiro chopatulika cha kudzipereka” [m’Chiheberi neʹzer, kuchokera ku mawu omwe aja akuti, na·zirʹ]. (Eks 39:30, 31) Komanso chisoti chachifumu chimene mafumu odzozedwa a Chiisiraeli ankavala chinkadziwikanso kuti neʹ-zer. (2Sa 1:10; 2Mf 11:12) Ponena za zomwe zimachitika mumpingo wa Chikhristu, mtumwi Paulo ananena kuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali m’malo mwa chovala kumutu. Tsitsili limamukumbutsa kuti malo ake ndi osiyana ndi a mwamuna ndipo amafunika kugonjera dongosolo la Mulungu. Choncho zimene Anaziri ankafunira kumachitazi, zomwe ndi kusameta tsitsi, kupeweratu kumwa vinyo komanso kukhala wosadetsedwa, zinkawakumbutsa kufunika kokhala odzimana ndiponso ogonjera zofuna za Yehova.—1Ak 11:2-16.