Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 49:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndodo yachifumu sidzachoka kwa Yuda,+ ndiponso chibonga cha wolamulira sichidzachoka pakati pa mapazi ake, mpaka Silo* atabwera.+ Ndipo mitundu ya anthu idzamumvera.+

  • 1 Mbiri 5:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Ngakhale kuti Yuda+ anali wamphamvu pakati pa azichimwene ake ndiponso kubanja lake kunachokera wodzakhala mtsogoleri,+ udindo wa woyamba kubadwa unali wa Yosefe.

  • Yesaya 9:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Chifukwa kwa ife kwabadwa mwana,+

      Ife tapatsidwa mwana wamwamuna,

      Ndipo ulamuliro* udzakhala paphewa pake.+

      Iye adzapatsidwa dzina lakuti Mlangizi Wodabwitsa,+ Mulungu Wamphamvu,+ Atate Wamuyaya, Kalonga Wamtendere.

  • Mateyu 2:4-6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Choncho Herode anasonkhanitsa ansembe aakulu ndi alembi onse a anthu, ndipo anawafunsa za kumene Khristu* adzabadwire. 5 Iwo anamuyankha kuti: “Adzabadwira ku Betelehemu+ wa ku Yudeya, chifukwa mneneri analemba zimenezi kuti: 6 ‘Iwe Betelehemu wamʼdziko la Yuda, si iwe mzinda waungʼono kwambiri kwa olamulira a Yuda, chifukwa mwa iwe mudzatuluka wolamulira amene azidzaweta anthu anga, Aisiraeli.’”+

  • Luka 1:32, 33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Ameneyu adzakhala wamkulu+ ndipo adzatchedwa Mwana wa Wamʼmwambamwamba.+ Yehova* Mulungu adzamupatsa mpando wachifumu wa Davide atate wake.+ 33 Iye adzalamulira monga Mfumu panyumba ya Yakobo kwamuyaya ndipo Ufumu wake sudzatha.”+

  • Luka 2:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chifukwa lero, mumzinda wa Davide+ mwabadwa mpulumutsi wanu,+ amene ndi Khristu Ambuye.+

  • Yohane 7:42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 42 Kodi si paja lemba limanena kuti Khristu adzachokera mwa ana a Davide+ komanso ku Betelehemu,+ mudzi umene Davide ankakhala?”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena