-
Yohane 2:1-11Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Pa tsiku lachitatu, ku Kana wa ku Galileya kunali phwando la ukwati ndipo mayi ake a Yesu analinso komweko. 2 Yesu ndi ophunzira ake anaitanidwanso kuphwando la ukwatilo.
3 Vinyo atatha, mayi ake a Yesu anamuuza kuti: “Vinyo wawathera.” 4 Koma Yesu anauza mayi akewo kuti: “Ndiye ife zikutikhudza bwanji mayi?* Nthawi yanga sinafike.” 5 Mayi akewo anauza amene ankatumikira kuti: “Muchite chilichonse chimene angakuuzeni.” 6 Pamalopo panali mbiya zamiyala zokwana 6, mogwirizana ndi malamulo a Ayuda a kudziyeretsa.+ Mbiya iliyonse inali ya malita pafupifupi 44 mpaka 66.* 7 Choncho Yesu anawauza kuti: “Dzazani mbiyazi ndi madzi.” Iwo anazidzazadi mpaka pakamwa. 8 Ndiyeno anawauza kuti: “Tsopano tunganimo pangʼono mukapereke kwa woyangʼanira phwandoli.” Iwo anakaperekadi. 9 Woyangʼanira phwando uja analawa madzi amene anawasandutsa vinyowo. Popeza kuti sanadziwe kumene wachokera (ngakhale kuti otumikira amene anatunga madziwo ankadziwa), woyangʼanira phwandoyo anaitana mkwati 10 nʼkumuuza kuti: “Munthu aliyense amatulutsa vinyo wabwino choyamba ndipo anthu akaledzera, mʼpamene amatulutsa wosakoma kwenikweni. Koma iwe wasunga vinyo wabwino mpaka nthawi ino.” 11 Yesu anachita zimenezi ku Kana wa ku Galileya monga chiyambi cha zizindikiro zake. Iye anaonetsa ulemerero wake+ ndipo ophunzira ake anayamba kumukhulupirira.
-