-
Baruki Mlembi Wokhulupirika wa YeremiyaNsanja ya Olonda—2006 | August 15
-
-
Usadzifunire “Zinthu Zazikulu”
Pamene ankalemba mpukutu woyambirira, Baruki anakumana ndi mavuto. Iye anadandaula kuti: “Kalanga ine tsopano! Pakuti Yehova wawonjezera chisoni pa zowawa zanga; ndalema ndi kubuula kwanga, sindipeza kupuma.” Kodi n’chifukwa chiyani zinthu zinafika pamenepa?—Yeremiya 45:1-3.
Palibe yankho lachindunji pa funso limeneli. Koma tangoyesani kuganiza za mmene Baruki analili. Kufotokoza za machenjezo opita kwa Israyeli ndi Yuda omwe anaperekedwa kwa zaka 23, kuyenera kuti kunapangitsa mpatuko wawo limodzinso ndi kukana kwawo Yehova kuonekera kwambiri. Baruki ayenera kuti anachita mantha ndi maganizo a Yehova oti awononge Yerusalemu ndi Yuda ndi kupititsa mtunduwo ku ukapolo wa ku Babulo kwa zaka 70, zinthu zimene Yehova ananena chaka chomwecho chimene Baruki analemba mpukutu woyambirira, ndipo mwina zimenezi zinalembedwanso mu mpukutuwo. (Yeremiya 25:1-11) Ndiponso, akanatha kutaya udindo ndi ntchito yake chifukwa chothandiza Yeremiya molimba mtima panthawi yovuta imeneyi.
Mulimonsemo, Yehova analowererapo kuti athandize Baruki kukumbukira za chiweruzo chimene chinali kubwera. Yehova anati: “Chimene ndamanga ndidzapasula, ndi chimene ndaoka ndidzazula; ndidzatero m’dziko lonseli.” Ndiyeno analangiza Baruki kuti: “Kodi udzifunira wekha zinthu zazikulu? Usazifune.”—Yeremiya 45:4, 5.
Yehova sanatchule kuti “zinthu zazikulu” zimenezi zinali chiyani, koma Baruki ayenera kuti ankadziwa kuti zinali zotani, mwina zadyera, kutchuka, kapena ulemerero wakuthupi. Yehova anam’patsa uphungu uwu kuti aone zinthu molondola ndiponso kuti asaiwale zimene zinali m’tsogolo: “Ndidzatengera zoipa pa anthu onse, . . . koma moyo wako ndidzakupatsa iwe ngati chofunkha m’malo monse mmene mupitamo.” Chinthu chofunika kwambiri chimene Baruki anali nacho, moyo wake, unasungidwa kulikonse kumene iye akanapita.—Yeremiya 45:5.
-
-
Baruki Mlembi Wokhulupirika wa YeremiyaNsanja ya Olonda—2006 | August 15
-
-
Baruki atakumbutsidwa kuti m’masiku otsiriza a Yuda, kunalibe nthawi yoti munthu azifuna “zinthu zazikulu,” zikuoneka kuti anamvera, chifukwa analandira moyo wake monga chofunkha. Tingachite bwino kutsatira uphungu umenewu, pamene tikukhala m’masiku otsiriza a dongosolo la zinthuli. Yehova watilonjeza zofanana ndi zimenezo, kuti moyo wathu udzapulumutsidwa. Kodi nafenso tingalabadire mawu otikumbutsa amenewo ngati mmene Baruki anachitira?
-