-
Kodi Yesu Anabadwa Liti Ndipo Anabadwira Kuti?Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Kaisara Augusito, yemwe anali mfumu ya Ufumu wa Roma, analamula kuti aliyense apite kwawo kuti akalembetse m’kaundula. Choncho Yosefe ndi Mariya anafunika kupita kwawo kumzinda wa Betelehemu, womwe unali kum’mwera kwa Yerusalemu.
Mzinda wa Betelehemu unadzaza ndi anthu amene anabwera kudzalembetsa m’kaundula. Chifukwa cha zimenezi, kunali kovuta kupeza malo ogona moti Yosefe ndi Mariya anapeza malo m’khola la abulu ndi nyama zina. Ndipo Yesu anabadwira m’kholamo. Atabadwa, Mariya anamukulunga m’nsalu ndipo anamugoneka mu chodyetsera nyamazo.
Mulungu ndi amene anachititsa kuti Kaisara Augusito apereke lamulo la kalemberayu. Tikutero chifukwa zimenezi zinachititsa kuti Yesu abadwire ku Betelehemu, womwe unali mzinda wa kwawo kwa Mfumu Davide. Malemba anali ataneneratu kukadali zaka zambiri kuti Wolamulira amene analonjezedwa adzabadwira mumzinda umenewu.—Mika 5:2.
-
-
Kodi Yesu Anabadwa Liti Ndipo Anabadwira Kuti?Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Masiku ano, anthu ambiri amakhulupirira kuti Yesu anabadwa pa 25 December. Koma ku Betelehemu, m’mwezi wa December kumakhala mvula komanso kumazizira kwambiri. Ndipo nthawi zina kumagwa sinoo. M’nyengo imeneyi, abusa sangakadyetse nkhosa zawo kutchire n’kumakagonera komweko. Komanso wolamulira wa Ufumu wa Roma sakanauza anthu, omwe sankasangalala kale ndi ulamuliro wake, kuti ayende m’nyengo yovutayi ulendo wa masiku angapo kukalembetsa. Choncho, pali umboni wosonyeza kuti Yesu anabadwa cha mu October.
-