Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 7. Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo abwino kwambiri

      Maboma a anthu amapanga malamulo omwe amayenera kuthandiza ndi kuteteza nzika zawo. Nawonso Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo amene nzika zake zimayenera kuwatsatira. Werengani 1 Akorinto 6:9-11, kenako mukambirane mafunso awa:

      • Kodi mukuganiza kuti zinthu zidzakhala bwanji padzikoli aliyense akamadzatsatira malamulo a Mulungu?a

      • Yehova amayembekezera kuti nzika za Ufumu wake zizitsatira malamulo ake, kodi mukuganiza kuti zimene Yehova amafunazi n’zoyenera? N’chifukwa chiyani mukutero?

      • Ndi mfundo iti imene ikusonyeza kuti anthu amene satsatira malamulo amenewa atha kusintha?​—Onani vesi 11.

      Wathirafiki akuimitsa magalimoto pamphambano ya msewu wodutsa anthu ambiri. Anthu amisinkhu yosiyanasiyana akuwoloka msewu.

      Maboma amakhazikitsa malamulo n’cholinga chofuna kuthandiza ndi kuteteza nzika zawo. Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo abwino kwambiri omwe amathandiza ndi kuteteza nzika zake

  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Kugonana?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • Yehova amafuna kuti zinthu zizitiyendera bwino. Iye amatiuza zimene tingachite kuti tikhale ndi makhalidwe oyera komanso ubwino wochita zimenezi. Werengani Miyambo 7:7-27 kapena onerani VIDIYO, kenako mukambirane mafunso otsatirawa.

      VIDIYO: Wopanda Nzeru Mumtima (9:31)

      • Kodi mnyamatayu anachita chiyani chomwe chikanatha kumulowetsa m’mayesero?​—Onani Miyambo 7:8, 9.

      • Lemba la Miyambo 7:23, 26, limasonyeza kuti kuchita chiwerewere kukhoza kutibweretsera mavuto aakulu. Ndiye kodi tingapewe mavuto ati tikamayesetsa kukhala ndi makhalidwe oyera?

      • Kodi kukhala ndi makhalidwe oyera kungatithandize bwanji kuti tizisangalala ndi moyo panopa mpaka kalekale?

      Anthu ena amaona kuti zimene Baibulo limanena pa nkhani ya kugonana kwa amuna komanso akazi okhaokha, ndi kukhwimitsa zinthu. Koma zimenezi si zoona chifukwa Yehova amatikonda ndipo amafuna kuti tonse tizisangalala ndi moyo panopa mpaka kalekale. Kuti zimenezi zitheke, tiziyesetsa kutsatira mfundo zake. Werengani 1 Akorinto 6:9-11, kenako mukambirane funso ili:

      • Kodi kugonana kwa amuna kapena akazi okhaokha ndi khalidwe lokhalo limene Mulungu amadana nalo?

      Kuti tizisangalatsa Mulungu, tonsefe tiyenera kuyesetsa kusintha moyo wathu. Kodi kuchita zimenezi n’kothandizadi? Werengani Salimo 19:8, 11, kenako mukambirane mafunso awa:

      • Kodi Yehova anachita bwino kutipatsa mfundo zamakhalidwe abwino kapena anangokhwimitsa zinthu? N’chifukwa chiyani mukutero?

      Zithunzi: 1. Mtsikana wakhala pafupi ndi chibwenzi chake ndipo akuoneka wosasangalala. Iye akumwa mowa komanso kusuta limodzi ndi anzake kumalo ena azisangalalo. 2. Mtsikana yemwe uja akucheza mosangalala ndi alongo ku Nyumba ya Ufumu.

      Yehova wathandiza anthu ambiri kuti asiye makhalidwe oipa. Inunso angakuthandizeni

  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Mowa?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 6. N’chiyani chimene chingathandize munthu kusiya kumwa mowa mopitirira malire?

      Onani zomwe zinathandiza munthu wina kusiya kumwa mowa mopitirira malire. Onerani VIDIYO, kenako mukambirane mafunso awa:

      VIDIYO: ‘Khalidwe Langa Loipa Linanditopetsa’ (6:32)

      Zithunzi: Zithunzi zamuvidiyo yakuti, ‘Khalidwe Langa Loipa Linanditopetsa.’ 1. Dmitry akuyang’ana botolo la mowa. 2. Dmitry, mkazi wake ndi mwana wawo akuphunzira Baibulo limodzi.
      • Kodi Dmitry ankatani akaledzera?

      • Kodi anakwanitsa kusiya kumwa mowa kamodzin’kamodzi?

      • N’chiyani chinamuthandiza kuti asiyiretu kumwa mowa mwauchidakwa?

      Werengani 1 Akorinto 6:10, 11, kenako mukambirane mafunso awa:

      • Kodi Baibulo limanena zotani pa nkhani ya kumwa mowa mwauchidakwa?

      • N’chiyani chikusonyeza kuti munthu yemwe amamwa mowa mopitirira malire akhoza kusintha?

      Werengani Mateyu 5:30, kenako mukambirane funso ili:

      • Pamene Yesu amanena za kudula dzanja ankatanthauza kuti tiyenera kulolera kusiya kuchita zinazake ndi cholinga choti tisangalatse Yehova. Kodi mungatani ngati zikukuvutani kusiya kumwa mowa mwauchidakwa?a

      Werengani 1 Akorinto 15:33, kenako mukambirane funso ili:

      • Kodi n’chiyani chimene chingakuchitikireni ngati mumacheza ndi anthu omwe amakonda kumwa mowa wambiri?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena