Kwa Agalatiya
2 Ndiyeno patapita zaka 14, ndinapitanso ku Yerusalemu limodzi ndi Baranaba, ndipo ndinatenganso Tito. 2 Ndinapita kumeneko cifukwa ca bvumbulutso limene ndinalandila, ndipo ndinafotokozela abalewo uthenga wabwino umene ndikuulalikila kwa anthu a mitundu ina. Ndinacita zimenezi mseli pamaso pa amuna odalilika, pofuna kutsimikizila kuti utumiki umene ndinali kucita kapena umene ndinali nditacita, usapite pacabe. 3 Ndipotu ngakhale kuti Tito amene ndinali naye anali Mgiriki, sanakakamizidwe kuti adulidwe. 4 Koma nkhani ya mdulidweyi inabuka cifukwa ca abale acinyengo amene analowa mwakacete-cete pakati pathu. Iwo analowa mozemba ngati akazitape kuti asokoneze ufulu umene tikusangalala nao mogwilizana ndi Khristu Yesu, n’colinga coti atigwile ukapolo. 5 Koma sitinawagonjele anthu amenewa ngakhale pang’ono kuti inu musataye coonadi ca uthenga wabwino.
6 Koma za aja amene anali kuoneka ngati ofunika kwambili, kaya anali otani, kwa ine zilibe kanthu, cifukwa Mulungu sayendela maonekedwe a munthu. Amuna odalilikawo sanaonjezele cidziwitso ciliconse catsopano mwa ine. 7 Komabe, iwo anaona kuti ndinapatsidwa nchito yolalikila uthenga wabwino kwa anthu osadulidwa, monga mmene Petulo anapatsidwila nchito yolalikila uthenga wabwino kwa anthu odulidwa. 8 Popeza amene anapatsa mphamvu Petulo kuti akhale mtumwi kwa anthu odulidwa, ndi amenenso anandipatsa mphamvu kuti ndikalalikile kwa anthu a mitundu ina. 9 Ndipo iwo atazindikila cisomo cimene ndinapatsidwa, Yakobo, Kefa,* ndi Yohane amene anali ngati mizati, anagwila canza ineyo ndi Baranaba poonetsa kuti agwilizana nazo zoti ife tipite kwa anthu a mitundu ina ndi kuti iwo apite kwa anthu odulidwa. 10 Koma iwo anangotipempha kuti tipitilize kukumbukila osauka, ndipo ndayesetsa kucita zimenezo moona mtima.
11 Koma Kefa* atabwela ku Antiokeya, ndinamutsutsa* pamasom’pamaso, cifukwa zinali zoonekelatu kuti anali wolakwa. 12 Zinali conco cifukwa anthu ena ocokela kwa Yakobo asanafike, iye anali kudya limodzi ndi anthu a mitundu ina. Koma iwo atafika, iye analeka kudya nao komanso kuceza nao poopa anthu odulidwa. 13 Ayuda enawo anayamba kucita naye zinthu zaciphamaso* zimenezi, moti nayenso Baranaba anayamba kucita nao zaciphamasozi.* 14 Koma nditaona kuti sakuyenda mogwilizana ndi coonadi ca uthenga wabwino, ndinauza Kefa* pamaso pa onse kuti: “Ngati iwe pokhala Myuda ukucita zinthu ngati anthu a mitundu ina, osati monga Myuda, n’cifukwa ciani ukulimbikitsa anthu a mitundu ina kuti azicita zinthu ngati Ayuda?”
15 Ife amene tinabadwa Ayuda, osati ocimwa ocokela m’mitundu ina, 16 timadziwa kuti munthu amayesedwa wolungama osati mwa kucita nchito za cilamulo, koma kokha mwa kukhulupilila Yesu Khristu. Conco, takhulupilila Khristu Yesu kuti tiyesedwe olungama cifukwa cokhulupilila iye, osati cifukwa ca nchito za cilamulo, cifukwa palibe munthu amene amayesedwa wolungama mwa kucita nchito za cilamulo. 17 Tsopano ngati ife tapezekanso kuti ndife ocimwa pamene tikuyesedwa olungama mwa Khristu, kodi ndiye kuti Khristu wakhala mtumiki wa ucimo? Kutalitali! 18 Ngati zinthu zomwezo zimene ndinagwetsa ndikuzimanganso, ndiye kuti ndikusonyeza kuti ndine wophwanya malamulo. 19 Koma cifukwa cakuti ndinali kutsatila cilamulo, ndinafa ku cilamulo kuti ndikhale ndi moyo n’kumatumikila Mulungu. 20 Ndinakhomeleledwa pamtengo limodzi ndi Khristu. Sindinenso amene ndikukhala ndi moyo, koma ndi Khristu amene akukhala ndi moyo mogwilizana ndi ine. Zoonadi, moyo umene ndikukhala tsopano, ndikukhala mokhulupilila Mwana wa Mulungu amene anandikonda n’kudzipeleka kaamba ka ine. 21 Sindikukana* kulandila cisomo ca Mulungu, cifukwa ngati munthu amayesedwa wolungama ndi nchito za cilamulo, ndiye kuti Khristu anafa pacabe.