LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 8
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Zopeleka zopita kwa Akhristu a ku Yudeya (1-15)

      • Tito atumizidwa ku Korinto (16-24)

2 Akorinto 8:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu Kabuku ka Misonkhano,

    5/2019, tsa. 3

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 209-210

2 Akorinto 8:12

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    12/1/2013, tsa. 17

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 8:1-24

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

8 Tsopano abale, tikufuna kuti mudziwe za cisomo cimene Mulungu wacitila mipingo ya ku Makedoniya. 2 Panthawi ya kusautsika kwao, ndi mayeso aakulu, iwo anakhala owolowa manja mwacimwemwe cosefukila, ngakhale kuti anali pa umphawi wadzaoneni. 3 Ndikucitila umboni kuti anapeleka malinga n’kupeza kwao kopelewelako, moti anacita zoposa pamenepo. 4 Iwo okha anacita kuticondelela kuti apatsidwe mwai wopeleka thandizo, kuti naonso aciteko utumiki wothandiza oyelawo. 5 Ndipo anathandizadi kuposa mmene tinali kuyembekezela. Coyamba anadzipeleka kwa Ambuye, kenako anadzipelekanso kwa ife mwa cifunilo ca Mulungu. 6 Conco tinalimbikitsa Tito kuti, popeza iye ndiye anayambitsa nchito yosonkhanitsa zopeleka zanu, iye ayenela kumalizitsanso nchito yotolela mphatso zanu zacifundo. 7 Inu mukucita bwino koposa pa ciliconse, monga pa cikhulupililo, luso la kulankhula, cidziwitso, pa khama, komanso mumakonda ena mmene ife timakukondelani. Conco, pa nkhani ya kupeleka, mucitenso cimodzi-modzi.

8 Sindikukamba izi mokulamulani ai, koma ndifuna kuti mudziwe za khama limene ena aonetsa, komanso kuti ndione ngati cikondi canu ndi ceniceni. 9 Pakuti mukudziwa cisomo ca Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemela, iye anakhala wosauka cifukwa ca inu, kuti kudzela mu umphawi wake, mukhale olemela.

10 Malangizo anga pamenepa ndi awa: Mungacite bwino kumalizitsa nchito ya zopelekayi imene munaiyamba caka catha cifukwa munaonetsa kale mtima wofunitsitsa kucita zimenezi. 11 Conco malizitsani nchito imene munaiyamba. Pakuti munali ofunitsitsa kucita zimenezi, mumalizitsenso kuzicita malinga ndi zimene muli nazo. 12 Mulungu amakondwela nayo mphatso yocokela pansi pa mtima, cifukwa Mulungu amafuna kuti munthu apeleke zimene angakwanitse, osati zimene sangakwanitse. 13 Sindikufuna kuti zinthu zikhale zopepuka kwa ena, koma zobvuta kwa inu. 14 Koma ndikufuna kuti zinthu zambili zimene muli nazo palipano, zithandizile pa zimene iwo alibe, komanso zinthu zambili zimene iwo ali nazo, zithandizile pa zimene inu mulibe kuti pakhale kufanana. 15 Monga mmene Malemba amakambila kuti: “Munthu amene anali ndi zambili sanakhale ndi zoculuka kupitilila muyeso, ndipo amene anali ndi zocepa, sanakhale ndi zocepa kwambili.”

16 Tikuyamika Mulungu pothandiza Tito kuti azikudelani nkhawa moona mtima monga mmene ifeyo timacitila. 17 Popeza iye walandila cilimbikitso cimene tinamupatsa, ndipo akufunitsitsa kuthandiza, akubwela kwa inu mwa kufuna kwake. 18 Koma tikumutumiza limodzi ndi m’bale wina amene mipingo yonse ikumutamanda cifukwa ca nchito zimene akucita zokhudzana ndi uthenga wabwino. 19 Cinanso, mipingo inasankha m’bale ameneyu kuti aziyenda nafe limodzi pamene tikupeleka mphatso zacifundozi kuti Ambuye alandile ulemelelo, komanso kuti tionetse kuti ndife okonzeka kuthandiza ena. 20 Conco, sitikufuna aliyense kutikaikila pa kayendetsedwe ka zopeleka zacifundo zoculukazi zimene tikubweletsa. 21 Tikucita zimenezi cifukwa ‘tikufuna kusamalila zinthu zonse moona mtima, osati pamaso pa Yehova pokha, koma ngakhale pamaso pa anthu.’

22 Abalewa tikuwatumizanso limodzi ndi m’bale wathu amene tamuyesa mobweleza-bweleza, ndipo waonetsa kuti ndi wakhama pa zinthu zambili. Panopa iye waonetsanso kuti ndi wakhama cifukwa amakudalilani kwambili. 23 Koma ngati mukumukaikila Tito pa ciliconse, ndikufuna ndikutsimikizileni kuti iye ndi mnzanga komanso wanchito mnzathu pokuthandizani. Ngatinso mukuwakaikila abale athu enawo, iwo ndi otumidwa ndi mipingo ndipo Khristu amalandila ulemelelo cifukwa ca iwo. 24 Conco aonetseni kuti mumawakonda, komanso onetsani mipingo cifukwa cake timakunyadilani.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani