Kalata Yoyamba kwa Atesalonika
4 Pomaliza abale, tinakupatsani malangizo a mmene muyenela kuyendela kuti muzikondweletsa Mulungu, ndipo n’zimenedi mukucita. Ndiye tikukupemphani komanso kukucondelelani m’dzina la Ambuye Yesu, kuti mupitilize kuonjezela kucita zimenezi. 2 Pakuti mukudziwa malangizo* amene tinakupatsani m’dzina la Ambuye Yesu.
3 Cifunilo ca Mulungu n’cakuti mukhale oyela ndiponso kuti muzipewa ciwelewele.* 4 Aliyense wa inu azidziwa kulamulila thupi lake kuti likhale loyela komanso lolemekezeka pamaso pa Mulungu. 5 Musakhale ngati anthu a mitundu ina omwe sadziwa Mulungu, amenenso ali ndi cilakolako cosalamulilika ca kugonana komanso dyela. 6 Pa nkhaniyi, pasapezeke wina aliyense wopitilila malile ake n’kudyela masuku pamutu m’bale wake, pakuti Yehova adzalanga munthu aliyense amene akucita zinthu zimenezi, monga mmene tinakuuzilani kale komanso kukucenjezani mwamphamvu. 7 Popeza Mulungu sanatiitane kuti tikhale ndi makhalidwe odetsa, koma kuti tikhale oyela. 8 Conco munthu amene akunyalanyaza macenjezo amenewa sakunyalanyaza munthu, koma Mulungu amene amakupatsani mzimu wake woyela.
9 Koma pa nkhani yokonda abale, m’posafunika kuti ticite kukulembelani, cifukwa Mulungu amakuphunzitsani kuti muzikondana. 10 Ndipo kunena zoona, inu mukucita kale zimenezi kwa abale onse a ku Makedoniya. Koma tikukulimbikitsani abale kuti mupitilize kucita zimenezi moposelapo. 11 Muziyesetsa kukhala mwamtendele. Musamalowelele nkhani za ena, ndipo muzigwila nchito ndi manja anu. Muzicita zimenezi malinga ndi malangizo amene tinakupatsani. 12 Muzicita zimenezi kuti anthu akunja aziona kuti mukuyenda bwino ndiponso kuti mukhale osasowa kanthu.
13 Cina abale, tikufuna kuti mudziwe za amene akugona mu imfa, kuti cisoni canu cisakhale ngati ca anthu ena amene alibe ciyembekezo. 14 Pakuti ngati timakhulupilila kuti Yesu anafa n’kuukitsidwa, ndiye kuti Mulungu adzaukitsanso amene akugona mu imfa kupyolela mwa Yesuyo, kuti akakhale naye* limodzi. 15 Zimene tikukuuzani malinga ndi mau a Yehova n’zakuti, ife amene tidzakhalabe ndi moyo mpaka pa nthawi ya kukhalapo kwa Ambuye, sitidzatsogola pa amene akugona mu imfa. 16 Pakuti Ambuye adzatsika kucokela kumwamba ndi mfuu yaulamulilo atanyamula lipenga la Mulungu. Mau ao adzamveka kuti ndi a mkulu wa angelo. Ndipo amene anafa mwa Khristu adzakhala oyambilila kuuka. 17 Kenako, ife amene tidzakhalebe amoyo limodzi ndi iwo, tidzatengedwa kupita m’mitambo kukakumana ndi Ambuye mumlengalenga, ndipo tizikakhala ndi Ambuyewo nthawi zonse. 18 Conco pitilizani kutonthozana ndi mau amenewa.