LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 8
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Nkhani yokhudza zakudya zopelekedwa kwa mafano (1-13)

        • Ife tili ndi Mulungu mmodzi yekha (5, 6)

1 Akorinto 8:1

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2018, masa. 12-16

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2017, tsa. 29

1 Akorinto 8:3

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2019, tsa. 12

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    7/2018, tsa. 8

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 8:1-13

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

8 Tsopano pa nkhani ya zakudya zopelekedwa kwa mafano, tikudziwa kuti tonse tili ndi cidziwitso. Cidziwitso cimapangitsa munthu kudzitukumula, koma cikondi cimamangilila. 2 Ngati wina akuganiza kuti akudziwa zinazake, ndiye kuti zinthuzo sanazidziwebe bwino. 3 Koma ngati munthu amakonda Mulungu, ndiye kuti munthuyo amadziwika kwa Mulungu.

4 Tsopano pa nkhani ya zakudya zopelekedwa kwa mafano, tikudziwa kuti fano ndi lopanda nchito m’dzikoli, ndipo kulibe Mulungu wina kupatulapo mmodzi yekhayo. 5 Pakuti ilipo yochedwa milungu kaya kumwamba kapena padziko lapansi. Ndipo ndi zoona, kuli “milungu” yambili ndi “ambuye” ambili. 6 Koma ife tili ndi Mulungu mmodzi yekha amene ndi Atate. Ndipo palinso Ambuye mmodzi, Yesu Khristu, amene zinthu zonse zinakhalapo kudzela mwa iye.

7 Komabe si onse amene amadziwa zimenezi. Koma cifukwa cakuti ena kale anali kulambila mafano, akamadya cakudyaco amaona ngati akudya cakudya copelekedwa kwa mafano. Ndipo cifukwa cakuti ndi ofooka, cikumbumtima cao cimawabvutitsa. 8 Cakudya sicingatithandize kuyandikila Mulungu. Ngati sitinadye, sikuti timakhala oipa ai, ndipo ngati tadya sikutinso timakhala abwino kwambili ai. 9 Koma samalani kuti ufulu wanu wosankha usakhale copunthwitsa mwa njila ina yake kwa amene ndi ofooka. 10 Ngati wina angakuone iwe wodziwa zinthu ukudya cakudya m’kacisi wa mafano, kodi cikumbumtima ca munthu wofooka sicidzamutuntha kuti adye zakudya zopelekedwa kwa mafano? 11 Conco cifukwa ca cidziwitso cako, cikhulupililo ca munthu wofookayo cidzaonongeka, m’bale wako amene Khristu anamufela. 12 Ngati mukucimwila abale anu mwa njila imeneyi ndi kubvulaza cikumbumtima cao cofooka, mukucimwila Khristu. 13 Ndiye cifukwa cake, ngati kudya nyama kukukhumudwitsa m’bale wanga, sindidzadyanso nyama ngakhale pang’ono, kuti ndisamukhumudwitse m’bale wanga.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani