LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 22
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Mawu a Paulo odziteteza pamaso pa khamu la anthu (1-21)

      • Paulo agwilitsa nchito unzika wake wokhala m’Roma (22-29)

      • Khoti Yaikulu ya Ayuda isonkhana (30)

Macitidwe 22:20

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “Pamene magazi a mboni yanu Stefano anali kukhetsedwa.”

Macitidwe 22:30

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “Sanihedirini.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 22:1-30

Macitidwe a Atumwi

22 “Amuna inu, abale ndi azitate, imvani mawu anga odziteteza.” 2 Ataona kuti akulankhula nawo m’Ciheberi, onse anangoti zii, ndipo iye anati: 3 “Ine ndine Myuda, wobadwila ku Tariso wa ku Kilikiya, koma ndinaphunzitsidwa ndi Gamaliyeli mu mzinda womwe uno. Anandiphunzitsa kutsatila mwakhama Cilamulo ca makolo athu. Ndinalinso wacangu kwambili potumikila Mulungu, ngati mmene zilili kwa nonsenu lelo. 4 Ndinali kuzunza otsatila Njilayo mpaka ena kuwapha. Ndinali kumanga amuna komanso akazi nʼkuwapeleka ku ndende. 5 Mkulu wa ansembe ndi bungwe lonse la akulu angandicitile umboni. Cifukwa kwa iwo n’kumene ndinatenga makalata ondiloleza kukamanga abale athu ku Damasiko. Ndinanyamuka kuti ndikagwile anthu a kumeneko nʼkuwapeleka ku Yerusalemu ali omangidwa kuti akapatsidwe cilango.

6 “Koma pamene ndinali mʼnjila, nditatsala pangʼono kufika ku Damasiko dzuwa lili pamutu, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kunandiunika. Kuwalaku kunacokela kumwamba ndipo kunandizungulila. 7 Ndiyeno ndinagwa pansi n’kumva mawu akuti: ‘Saulo! Saulo! N’cifukwa ciyani ukundizunza?’ 8 Ine ndinayankha kuti: ‘Ambuye, kodi ndinu ndani?’ Iye anandiuza kuti: ‘Ndine Yesu Mnazareti amene ukumuzunza.’ 9 Anthu amene ndinali nawo anaona kuwalako, koma sanamve mawu a amene anali kulankhula nane. 10 Ndiyeno ine ndinati, ‘Ndicite ciyani Ambuye?’ Ambuyewo anandiuza kuti, ‘Nyamuka upite ku Damasiko. Kumeneko udzauzidwa zonse zimene zakonzedwa kuti ucite.’ 11 Koma popeza sindinali kutha kuona cifukwa ca mphamvu ya kuwalako, anthu amene ndinali nawo anandigwila dzanja mpaka kukafika ku Damasiko.

12 “Ndiyeno munthu wina woopa Mulungu mogwilizana ndi Cilamulo, dzina lake Hananiya, amene anali ndi mbili yabwino pakati pa Ayuda okhala kumeneko, 13 anabwela. Anaima pafupi ndi ine n’kundiuza kuti: ‘Saulo m’bale wanga, yambanso kuona!’ Nthawi yomweyo ndinakweza maso anga n’kumuona. 14 Ndiyeno anandiuza kuti: ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha kuti udziwe cifunilo cake, komanso kuti uone wolungamayo ndi kumva mawu otuluka pakamwa pake. 15 Cifukwa udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zinthu zimene waona ndi kumva. 16 Ndiye n’cifukwa ciyani ukuzengeleza? Nyamuka ubatizike n’kucotsa macimo ako mwa kuitanila pa dzina lake.’

17 “Koma pamene ndinabwelela ku Yerusalemu n’kuyamba kupemphela m’kacisi, ndinaona masomphenya. 18 M’masomphenyawo ndinaona Ambuye akundiuza kuti: ‘Tuluka mwamsanga mu Yerusalemu, cifukwa anthuwo sadzamvela uthenga umene ukulengeza wokhudza ine.’ 19 Ndipo ine ndinati: ‘Ambuye, iwowa akudziwa bwino kuti ndinali kupita m’masunagoge n’kumaika anthu m’ndende, ndi kukwapula amene amakukhulupililani. 20 Pamene Sitefano mboni yanu anali kuphedwa,* ineyo ndinalipo, ndipo ndinavomelezana nazo. Ine ndi amene ndinali kuyang’anila zovala zakunja za anthu amene anali kumupha.’ 21 Koma iye anandiuza kuti: ‘Pita, cifukwa ndidzakutumiza kutali kwa anthu a mitundu ina.’”

22 Iwo anali kumumvetsela mpaka atanena mawu amenewa. Ndiyeno anafuula kuti: “M’cotseni munthu ameneyu pa dziko lapansi! Cifukwa sayenela kukhala ndi moyo!” 23 Popeza anali kufuula komanso kumaponya zovala zawo zakunja ndi fumbi m’mwamba, 24 mkulu wa asilikali analamula kuti Paulo alowe naye kumalo okhala asilikali. Ndipo anati ayenela kumufunsa mafunso kwinaku akum’kwapula kuti adziwe cimene anthu anali kumukuwilila conci. 25 Koma atamugoneka kuti amukwapule, Paulo anafunsa woyang’anila asilikali amene anaima pafupi naye kuti: “Kodi malamulo amakulolani kukwapula nzika ya Roma mlandu wake usanazengedwe?” 26 Mtsogoleli wa asilikaliyo atamva zimenezo, anapita kwa mkulu wa asilikali nʼkumuuza kuti: “Kodi mukufuna kucita ciyani? Pakuti munthuyu ndi nzika ya Roma.” 27 Conco mkulu wa asilikaliyo anayandikila Paulo n’kumufunsa kuti: “Ndiuze, kodi ndiwe nzika ya Roma?” Iye anati: “Inde.” 28 Mkulu wa asilikaliyo anakamba kuti: “Ine ndinagula ufulu wokhala nzika ya Roma ndi ndalama zambili.” Paulo anati: “Koma ine ndinacita kubadwa nawo.”

29 Nthawi yomweyo amuna amene anali kufuna kumufunsa mafunso kwinaku akumukwapula, anamutalamuka. Ndipo mkulu wa asilikaliyo anacita mantha atazindikila kuti munthu amene anamumanga uja ndi nzika ya Roma.

30 Conco tsiku lotsatila, popeza anali kufuna kudziwa cimene Ayuda anali kumuimbila mlandu, anamumasula. Ndiyeno analamula kuti ansembe aakulu komanso onse a m’Bungwe Lalikulu la Ayuda* asonkhane. Kenako anabweletsa Paulo nʼkumuimika pakati pawo.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani