LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 18
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Utumiki wa Paulo ku Korinto (1-17)

      • Abwelela ku Antiokeya wa ku Siriya (18-22)

      • Paulo acoka n’kupita ku Galatiya ndi ku Filigiya (23)

      • Apolo wolankhula mwaluso athandizidwa (24-28)

Macitidwe 18:7

Mawu amunsi

  • *

    Kutanthauza ku sunagoge.

Macitidwe 18:12

Mawu amunsi

  • *

    Kutanthauza bwanamkubwa wa cigawo ca Roma.

Macitidwe 18:22

Mawu amunsi

  • *

    Zioneka kuti anapita ku Yerusalemu.

Macitidwe 18:25

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “anaphunzitsidwa ndi mawu apakamwa.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 18:1-28

Macitidwe a Atumwi

18 Pambuyo pake Paulo anacoka ku Atene n’kupita ku Korinto. 2 Kumeneko anapeza Myuda wina dzina lake Akula, wa ku Ponto. Iye ndi mkazi wake Purisila, anali atangofika kumene kucokela ku Italy, cifukwa Kalaudiyo anali atalamula kuti Ayuda onse acoke ku Roma. Conco Paulo anapita kunyumba kwawo. 3 Popeza nchito yawo inali yofanana, anakhala kunyumba kwawo. Iwo anali kugwilila nchito pamodzi cifukwa onse anali opanga matenti. 4 Paulo anali kukamba nkhani m’sunagoge sabata lililonse, ndipo anali kukopa Ayuda ndi Agiriki.

5 Tsopano Sila ndi Timoteyo atafika kucokela ku Makedoniya, Paulo anatangwanika kwambili ndi nchito yolalikila mawu a Mulungu. Iye anali kucitila umboni kwa Ayuda ndiponso kuwatsimikizila kuti Yesu ndiye Khristu. 6 Koma iwo atapitiliza kumutsutsa komanso kumunyoza, iye anakutumula zovala zake n’kuwauza kuti: “Magazi anu akhale pa mutu panu. Ine ndilibe mlandu. Kuyambila tsopano ndizipita kwa anthu a mitundu ina.” 7 Conco, iye anacoka kumeneko* n’kupita kunyumba ya munthu wina dzina lake Titiyo Yusito. Iye anali munthu wolambila Mulungu, amene nyumba yake inali moyandikana ndi sunagoge. 8 Kirisipo, mtsogoleli wa sunagoge, anakhala wokhulupilila Ambuye, pamodzi ndi anthu onse a m’banja lake. Anthu ambili a ku Korinto amene anamva uthenga wabwino, anayamba kukhulupilila ndipo anabatizika. 9 Koma usiku Ambuye anauza Paulo m’masomphenya kuti: “Usaope, pitiliza kulankhula. Ndipo usakhale cete, 10 cifukwa ine ndili nawe. Ndipo palibe amene adzakupanda kapena kukucita zacipongwe, popeza ndili ndi anthu ambili mu mzindawu.” 11 Conco anakhala kumeneko caka cimodzi ndi miyezi 6, akuwaphunzitsa mawu a Mulungu.

12 Pamene Galiyo anali bwanamkubwa* wa Akaya, Ayuda anagwilizana zogwila Paulo, ndipo anapita naye ku mpando woweluzila milandu. 13 Kumeneko iwo anati: “Munthu uyu akukopa anthu kuti azipembedza Mulungu m’njila yosemphana ndi Cilamulo.” 14 Koma Paulo atangotsala pang’ono kuyamba kulankhula, Galiyo anauza Ayudawo kuti: “Inu Ayuda, cikanakhala colakwa cina kapena mlandu waukulu, ndithu ndikanaleza mtima kukumvetselani. 15 Koma ngati nkhani yake ndi yokhudza mikangano pa mawu, maina ndi cilamulo canu, muthane nazo nokha. Sindikufuna kuti ndikhale woweluza pa nkhani ngati zimenezi.” 16 Atatelo, anauza anthuwo kuti acoke ku mpando woweluzila milanduwo. 17 Zitatelo, onse anagwila Sositeni mtsogoleli wa sunagoge n’kuyamba kumumenya pafupi ndi mpando woweluzila milanduwo. Koma Galiyo sanafune kulowelelapo ngakhale pang’ono pa zinthu zimenezi.

18 Paulo atakhala kumeneko kwa masiku ndithu, analayilana ndi abalewo n’kunyamuka ulendo wa panyanja kupita ku Siriya. Pa ulendowu anapita limodzi ndi Purisila ndi Akula. Paulo ali ku Kenkereya, anameta tsitsi lake cifukwa ca lumbilo limene anacita. 19 Conco iwo anafika ku Efeso, ndipo anasiya anzakewo kumeneko. Koma iye anapita kukalowa m’sunagoge n’kuyamba kukambilana ndi Ayuda. 20 Ngakhale kuti iwo mobwelezabweleza anamupempha kuti akhale nawo kwa masiku ena ambili, iye sanalole. 21 M’malomwake, analayilana nawo n’kuwauza kuti: “Yehova akalola, ndidzabwelanso kudzakuonani.” Kenako ananyamuka ku Efeso n’kuyamba ulendo wa panyanja, 22 ndipo anafika ku Kaisareya. Kenako anapita* kukapeleka moni ku mpingo, ndipo pambuyo pake anapita ku Antiokeya.

23 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, ananyamuka n’kuyamba kuyenda malo osiyanasiyana m’cigawo ca Galatiya ndi Fulugiya, ndipo anali kulimbikitsa ophunzila onse.

24 Tsopano Myuda wina dzina lake Apolo wa ku Alekizandiriya, anafika ku Efeso. Ameneyu anali kulankhula mwaluso komanso anali kudziwa bwino Malemba. 25 Mwamuna ameneyu anaphunzitsidwa* njila ya Yehova. Anali wodzipeleka kwambili cifukwa anali ndi mzimu woyela, ndipo anali kulankhula ndi kuphunzitsa za Yesu molondola. Koma iye anali kudziwa za ubatizo wa Yohane wokha basi. 26 Iye anayamba kulankhula molimba mtima m’sunagoge. Ndiyeno Purisila ndi Akula atamumvetsela, anamutenga n’kumufotokozela njila ya Mulungu molondola. 27 Ndipo popeza kuti Apolo anali kufunitsitsa kupita ku Akaya, abalewo analembela kalata ophunzila kumeneko. Anawalimbikitsa kuti amulandile bwino. Conco iye atafika kumeneko, anawathandiza kwambili anthu amene mwa cisomo ca Mulungu, anakhala okhulupilila. 28 Cifukwa iye anawatsimikizila Ayuda poyela komanso mwamphamvu kuti anali olakwa. Ndipo anagwilitsa nchito Malemba poonetsa kuti Yesu ndiye Khristu.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani