LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 25
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Paulo afotokoza mlandu wake pamaso pa Fesito (1-12)

        • “Ndikucita apilo kuti ndikaonekele kwa Kaisara!” (11)

      • Fesito afunsila nzelu kwa Mfumu Agiripa (13-22)

      • Paulo aonekela pamaso pa Agiripa (23-27)

Macitidwe 25:11

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2016, masa. 15-16

Macitidwe 25:19

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “yokhudza cipembedzo cawo.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 25:1-27

Macitidwe a Atumwi

25 Fesito anafika m’cigawoco n’kuyamba kulamulila. Patapita masiku atatu ananyamuka ku Kaisareya n’kupita ku Yerusalemu. 2 Kumeneko, ansembe aakulu ndi amuna olemekezeka pakati pa Ayuda anamuuza zinthu zoipa zokhudza Paulo. Conco iwo anayamba kucondelela Fesito 3 kuti awakomele mtima n’kuitanitsa Paulo kuti abwele ku Yerusalemu. Koma anakonza zakuti abisalile Paulo panjila kuti amuphe. 4 Koma Fesito anawayankha kuti Paulo ayenela kusungidwila ku Kaisareya, komanso kuti iye watsala pang’ono kubwelela kumeneko. 5 Iye anati, “Amene ali ndi ulamulilo pakati panu, apite nane limodzi kuti akamuimbe mlandu munthu uyu ngati pali cimene analakwa.”

6 Conco iye atakhala nawo masiku osapitilila 8 kapena 10, anabwelela ku Kaisareya. Tsiku lotsatila anakhala pa mpando woweluzila milandu n’kulamula anthu kuti abweletse Paulo kwa iye. 7 Paulo atafika, Ayuda amene anabwela kucokela ku Yerusalemu anaimilila momuzungulila, ndipo anayamba kumuneneza milandu yambili ikuluikulu imene sanathe kupeleka umboni wake.

8 Koma Paulo podziteteza anati: “Ine sindinacimwile Cilamulo ca Ayuda, kapena kacisi, kapenanso Kaisara.” 9 Pofuna kukondweletsa Ayuda, Fesito anafunsa Paulo kuti: “Kodi ungakonde kupita ku Yerusalemu kuti nkhani yako ikaweluzidwile kumeneko pamaso panga?” 10 Koma Paulo anayankha kuti: “Ine ndaimilila patsogolo pa mpando woweluzila milandu wa Kaisara pamene ndiyenela kuweluzidwa. Ayuda sindinawalakwile ciliconse, ndipo inunso mukuona zimenezi. 11 Ngati ndinalakwadi, ndipo ndinacita ciliconse coyenela imfa, sindikukana kufa. Koma ngati anthu awa alibe umboni pa zimene akundinenezazi, palibe munthu amene ali ndi ufulu wondipeleka kwa iwo pofuna kuwasangalatsa. Conco ndikucita apilo kuti ndikaonekele kwa Kaisara!” 12 Ndiyeno Fesito atakambilana ndi bungwe la akulu, anayankha kuti, “Popeza wacita apilo kwa Kaisara, udzapitadi kwa Kaisara.”

13 Patapita masiku angapo, Mfumu Agiripa ndi Berenike anafika ku Kaisareya kudzaona Fesito. 14 Popeza iwo anakhala kumeneko kwa masiku ndithu, Fesito anafotokozela mfumuyo nkhani ya Paulo. Anati:

“Pali munthu wina amene Felike anamusiya m’ndende. 15 Ndipo pamene ndinali ku Yerusalemu, ansembe aakulu ndi akulu a Ayuda anandiuza zoipa zokhudza munthuyu. Ndipo iwo anapempha kuti iye alandile ciweluzo cakuti aphedwe. 16 Koma ine ndinawayankha kuti Aroma sapeleka munthu kwa omuneneza pofuna kuwakondweletsa munthuyo asanakumane ndi omunenezawo pamasom’pamaso kuti adziteteze pa mlanduwo. 17 Conco atafika kuno sindinacedwe. Tsiku lotsatila ndinakhala pa mpando woweluzila milandu n’kulamula kuti munthuyo amubweletse kwa ine. 18 Omunenezawo ataimilila n’kuyamba kufotokoza, sananene zoipa zilizonse zimene ndinali kuganiza kuti munthuyu anacita. 19 Iwo anangotsutsana naye pa nkhani yokhudza mmene amalambilila Mulungu,* komanso za munthu wina dzina lake Yesu amene anafa. Koma Paulo amanenabe motsimikiza kuti ali moyo. 20 Nditalephela kupeza njila ya mmene ndingathetsele mkangano wa nkhani zimenezi, ndinamufunsa ngati angakonde kuti apite ku Yerusalemu kuti akaweluzidwile kumeneko. 21 Koma Paulo atapempha kuti timusungebe m’ndende kuti cigamulo cikapelekedwe ndi Mfumu yaikulu, ndinalamula kuti asungidwebe kufikila nditamutumiza kwa Kaisara.”

22 Ndiyeno Agiripa anauza Fesito kuti: “Ndingakonde kuti ndimve ndekha pamene munthuyu akulankhula.” Iye anati: “Mudzamumvetsela mawa.” 23 Conco tsiku lotsatila, Agiripa ndi Berenike anabwela ndi ulemelelo waukulu n’kulowa m’bwalo limene munali anthu pamodzi ndi akuluakulu a asilikali komanso anthu ochuka a mu mzindamo. Ndipo Fesito atalamula kuti Paulo abwele kwa iye, anamubweletsa. 24 Kenako Fesito anakamba kuti: “Mfumu Agiripa ndi nonsenu amene muli nafe pano, munthu uyu amene mukumuona ndi amene Ayuda onse ku Yerusalemu ndi kuno komwe, anandipempha kuti sakuyenelelanso kukhalabe ndi moyo, ndipo iwo anali kunena izi mofuula. 25 Koma ndinaona kuti sanalakwe ciliconse kuti ayenelele kuphedwa. Conco munthuyu atapempha kuti akaonekele kwa Mfumu yaikulu, ndinaganiza zomutumiza. 26 Koma ndilibe mfundo iliyonse yomveka imene ndingalembele Mbuye wanga yokhudza munthuyu. Conco ndamubweletsa kwa nonsenu, makamaka kwa inu Mfumu Agiripa, kuti akafunsidwa mafunso ndipeze colemba. 27 Cifukwa ndikuona kuti si canzelu kutumiza mkaidi, koma osachula milandu yake.”

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani