LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 7
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Malangizo kwa anthu osakwatila komanso kwa okwatila (1-16)

      • Mukhalebe mmene munalili pamene Mulungu anakuitanani (17-24)

      • Anthu osakwatila komanso akazi amasiye (25-40)

        • Ubwino wokhala mbeta (32-35)

        • Kukwatila “kokha mwa Ambuye” (39)

1 Akorinto 7:1

Mawu amunsi

  • *

    Kutanthauza kugonana.

1 Akorinto 7:2

Mawu amunsi

  • *

    M’Cigiriki ndi por·nei′a. Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 7:3

Mawu amunsi

  • *

    Kutanthauza nkhani za kugonana.

1 Akorinto 7:5

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    1/15/2015, tsa. 27

1 Akorinto 7:10

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, masa. 13-14

1 Akorinto 7:11

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, masa. 13-14

1 Akorinto 7:13

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, tsa. 14

1 Akorinto 7:14

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2016, tsa. 16

1 Akorinto 7:15

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “kupatukana ndi mnzake; kusalana ndi mnzake.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2016, masa. 16-17

1 Akorinto 7:25

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “anamwali.”

1 Akorinto 7:28

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    7/2020, tsa. 3

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    6/2017, masa. 4-6

    Nsanja ya Mlonda,

    1/15/2015, masa. 18-19

1 Akorinto 7:29

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2016, tsa. 17

1 Akorinto 7:31

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2016, tsa. 17

    Nsanja ya Mlonda,

    10/15/2015, masa. 17-18

1 Akorinto 7:32

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

1 Akorinto 7:33

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

1 Akorinto 7:35

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “kukumangani mu khwekhwe kapena kuti gango.”

1 Akorinto 7:36

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

1 Akorinto 7:37

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “kusungabe unamwali wake.”

1 Akorinto 7:38

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

1 Akorinto 7:39

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, masa. 134-135

    Nsanja ya Mlonda,

    3/15/2015, masa. 30-32

    1/15/2015, masa. 31-32

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
  • 38
  • 39
  • 40
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 7:1-40

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

7 Tsopano pa nkhani ija imene munandilembela, zingakhale bwino kuti mwamuna asakhudze* mkazi. 2 Koma cifukwa ca kuculuka kwa ciwelewele,* mwamuna aliyense akhale ndi mkazi wake-wake, ndipo mkazi aliyense akhale ndi mwamuna wake-wake. 3 Mwamuna azipeleka mangawa kwa mkazi wake,* mkazinso azipeleka mangawa kwa mwamuna wake. 4 Mkazi alibe ulamulilo pathupi lake. Koma amene ali ndi ulamulilo ndi mwamuna wake. Mwamuna nayenso alibe ulamulilo pathupi lake, koma mkazi wake ndi amene ali ndi ulamulilo. 5 Musamakanizane, kupatulapo ngati mwacita kugwilizana kuti muimitse kwa kanthawi kuti mugwilitse nchito nthawiyo kupemphela. Pambuyo pake n’kuyambanso mwa nthawi zonse. Muzitelo kuti Satana asapitilize kukuyesani mukalephela kudziletsa. 6 Ndalankhula izi osati monga lamulo, koma kuti mudziwe zimene zili zololeka. 7 Ndikanakonda amuna onse akanakhala ngati ine. Ngakhale n’telo, munthu wina aliyense ali ndi mphatso imene Mulungu anamupatsa, wina m’njila iyi winanso m’njila ina.

8 Tsopano ndikuuza anthu osakwatila komanso akazi amasiye kuti zingakhale bwino kwa iwo kupitiliza kukhala mmene ine ndilili. 9 Koma ngati sangakwanitse kudziletsa akwatile, cifukwa kukwatila kuli bwino kusiyana n’kumabvutika ndi cilakolako.

10 Kwa anthu okwatila ndikupeleka malangizo awa, osati ine koma Ambuye, kuti mkazi asasiye mwamuna wake. 11 Koma ngati angamusiye, mkaziyo akhalebe wosakwatiwa. Apo ai, abwelelane ndi mwamuna wake. Nayenso mwamuna asasiye mkazi wake.

12 Koma kwa enawo, ineyo osati Ambuye, ndikuwauza kuti: Ngati m’bale ali ndi mkazi wosakhulupilila, ndipo akulola kukhala naye, asamusiye mkaziyo. 13 Komanso ngati mkazi ali ndi mwamuna wosakhulupilila, ndipo akulola kukhala naye, asamusiye mwamunayo. 14 Pakuti mwamuna wosakhulupilila amayeletsedwa cifukwa ca mkazi wake. Ndipo mkazi wosakhulupilila amayeletsedwa cifukwa ca m’baleyo. Apo ai, ana anu akanakhala odetsedwa, koma tsopano ndi oyela. 15 Koma ngati wosakhulupililayo wasankha kucoka,* mulekeni acoke. Zikakhala telo, m’bale kapena mlongo sakhala womangika, koma Mulungu wakuitanani kuti mukhale mwamtendele. 16 Mkaziwe, udziwa bwanji kuti mwina ungapulumutse mwamuna wako? Kapenanso mwamunawe, udziwa bwanji kuti mwina ungapulumutse mkazi wako?

17 Ngakhale n’telo, munthu aliyense akhalebe mmene analili pamene Yehova Mulungu anamuitana. Conco ndikupeleka malangizo awa ku mipingo yonse. 18 Kodi pali mwamuna amene anaitanidwa ali wodulidwa? Akhalebe conco wodulidwa. Kodi pali mwamuna amene anaitanidwa ali wosadulidwa? Ameneyo asadulidwe. 19 Mdulidwe, kapena kukhala wosadulidwa zilibe tanthauzo lililonse. Koma cofunika ndi kusunga malamulo a Mulungu. 20 Munthu aliyense akhalebe mmene analili pomwe anaitanidwa. 21 Kodi unaitanidwa uli kapolo? Zimenezo zisakudetse nkhawa. Koma ngati ungakhale ndi mwai womasuka, ugwilitse nchito mwai umenewo. 22 Munthu aliyense amene anaitanidwa mwa Ambuye ali kapolo ndi mtumiki womasulidwa wa Ambuye. Mofananamo, aliyense amene anaitanidwa ali mfulu ndi kapolo wa Khristu. 23 Munagulidwa pa mtengo wodula, lekani kukhala akapolo a anthu. 24 Abale, munthu aliyense akhalebe mmene analili pomwe anaitanidwa ndi Mulungu.

25 Ponena za amene sanakwatiwepo* kapena kukwatilapo, ndilibe lamulo lililonse la Ambuye. Koma ndikupeleka malingalilo anga ngati munthu amene anacitilidwa cifundo ndi Ambuye kuti ndikhale wokhulupilika. 26 Conco, ndiganiza kuti zingakhale bwino kuti mwamuna akhalebe mmene alili cifukwa ca kubvuta kwa zinthu palipano. 27 Kodi ndiwe womangika kwa mkazi? Leka kufuna-funa njila yomasukila. Kodi ndiwe womasuka kwa mkazi? Leka kufuna-funa mkazi. 28 Koma ngati ungakwatile, sikuti wacimwa ai. Ndipo ngati munthu amene sali pabanja walowa m’banja, munthuyo sanacimwe ai. Komabe amene alowa m’banjawo adzakhala ndi nsautso m’matupi ao. Koma ndikungoyesa kukutetezani.

29 Komanso, ndikukuuzani izi abale: Nthawi yotsalayi yafupika. Kuyambila tsopano, amene ali ndi akazi azikhala ngati amene alibe, 30 ndipo amene akulila azikhala ngati aja amene sakulila, amene akusangalala azikhala ngati amene sakusangalala, ndipo amene amagula zinthu azikhala ngati amene alibe kanthu. 31 Amene akuligwilitsa nchito dzikoli azikhala ngati amene sakuligwilitsa nchito mokwanila cifukwa zocitika pa dzikoli zikusintha. 32 Kukamba zoona, ndikufuna kuti mukhale opanda nkhawa. Mwamuna wosakwatila amadela nkhawa za Ambuye, mmene angakhalile woyanjidwa ndi Ambuye. 33 Koma mwamuna wokwatila amadela nkhawa zinthu za dziko mmene angakondweletsele mkazi wake, 34 ndipo amakhala wogawikana. Nayenso mkazi wosakwatiwa komanso namwali, amadela nkhawa zinthu za Ambuye kuti thupi ndi maganizo ake zikhale zoyela. Koma mkazi wokwatiwa amadela nkhawa zinthu za dziko mmene angakondweletsele mwamuna wake. 35 Ndikukamba izi kaamba ka ubwino wanu, osati kuti ndikupanikizeni* ai, koma kuti ndikulimbikitseni kucita zoyenela, komanso kuti nthawi zonse mukhale odzipeleka kwa Ambuye popanda cosokoneza.

36 Koma ngati wina amene sali pa banja akulephela kuugwila mtima cifukwa ca cilakolako, ndipo munthuyo wapitilila cimake ca unyamata, zimene ziyenela kucitika ndi izi, mulekeni akwatile ngati n’zimene akufuna, iye sakucimwa. 37 Koma ngati wina watsimikiza mumtima mwake, ndipo sakuona cifukwa colowela m’banja, komanso akutha kulamulila cilakolako cake, komanso mumtima mwake wasankha kukhalabe wosakwatila,* wacita bwino. 38 Nayenso amene wakwatila wacita bwino. Koma amene wacita bwino kwambili ndi amene sanakwatile.

39 Mkazi amakhala womangika pa nthawi yonse imene mwamuna wake ali moyo. Koma ngati mwamuna wake wamwalila, amakhala womasuka kukwatiwanso kwa aliyense amene wafuna, koma kokha mwa Ambuye. 40 Koma ndikuona kuti mkaziyo angakhale wacimwemwe kwambili ngati angakhalebe mmene alili. Ndipo sindikukaikila kuti pamenepa ndilinso ndi mzimu wa Mulungu.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani