Kwa Agalatiya
3 Agalatiya opusa inu! Ndani anakupotozani maganizo, inu amene munakhala ngati mwaona Yesu Khristu atam’khomelela pamtengo? 2 Ndifuna ndikufunseni* funso limodzi ili: Kodi munalandila mzimu cifukwa cocita nchito za cilamulo, kapena cifukwa cokhulupilila zimene munamva? 3 Kani ndinu opusa conci? Inu munayamba ndi nchito za mzimu, kodi mukufuna kutsiliza ndi nchito za thupi? 4 Kodi kubvutika konse kuja kunangopita pacabe? Ndikukhulupilila kuti sikunapite pacabe. 5 Cotelo, amene amakupatsani mzimu ndi kucita nchito zamphamvu* pakati panu, kodi amatelo cifukwa cakuti mumacita nchito za cilamulo kapena cifukwa cakuti munakhulupilila zimene munamva? 6 N’cimodzi-modzinso Abulahamu, iye “anakhulupilila mwa Yehova ndipo anamuyesa wolungama.”
7 Inu mukudziwa bwino kuti anthu okhawo amene ali ndi cikhulupililo ndiwo ana a Abulahamu. 8 Malemba anakambilatu kuti Mulungu adzaona anthu a mitundu ina kukhala olungama cifukwa ca cikhulupililo. Ndipo Mulungu analengezelatu uthenga wabwino kwa Abulahamu wakuti: “Kudzela mwa iwe, anthu a mitundu yonse adzadalitsidwa.” 9 Conco amene ali ndi cikhulupililo akudalitsidwa limodzi ndi Abulahamu, munthu amene anali ndi cikhulupililo.
10 Onse amene amadalila nchito za cilamulo ndi otembeleledwa, cifukwa Malemba amati: “Wotembeleledwa ndi aliyense amene satsatila zonse zolembedwa mu mpukutu wa Cilamulo.” 11 Ndiponso, n’zodziwikilatu kuti kulibe munthu amene Mulungu amamuyesa wolungama cifukwa ca cilamulo, pakuti “wolungama adzakhala ndi moyo cifukwa ca cikhulupililo cake.” 12 Tsopano maziko a Cilamulo si cikhulupililo. Koma “aliyense amene akucita nchito za m’Cilamulo adzakhala ndi moyo cifukwa ca cilamuloco.” 13 Khristu anatigula n’kutimasula ku tembelelo la Cilamulo. Anatelo mwa kukhala tembelelo m’malo mwa ife, pakuti Malemba amati: “Wotembeleledwa ndi aliyense amene wapacikidwa pamtengo.” 14 Iye anatelo n’colinga cakuti madalitso amene analonjezedwa kwa Abulahamu abwele kwa anthu a mitundu ina kudzela mwa Khristu Yesu. Zinatelo kuti ndi cikhulupililo, tilandile mzimu wolonjezedwawo.
15 Abale anga, ndiloleni ndifotokoze fanizo la zimene zimacitikila anthu: Cipangano cikakhazikitsidwa, ngakhale kuti n’capakati pa anthu, palibe amene angacithetse kapena kuonjezelamo mfundo zina. 16 Tsopano malonjezowo ananenedwa kwa Abulahamu ndi kwa mbadwa* yake. Malemba sanena kuti, “ndi kwa mbadwa* zako,” monga kuti mbadwazo n’zambili ai. M’malomwake, Malemba amati, “ndi kwa mbadwa* yako,” kutanthauza munthu mmodziyo, Khristu. 17 Zimene ndikutanthauza ine ndi izi: Mulungu anacita cipangano ndi Abulahamu, ndipo patapita zaka 430, anapeleka cilamulo kwa anthu ake. Koma zimenezi sizinaphwanye cipangano cimene Mulungu anacita ndi Abulahamu, moti n’kulepheletsa lonjezolo kugwila nchito. 18 Pakuti ngati colowa cidalila cilamulo, ndiye kuti colowaco sicidalila lonjezo. Koma Mulungu mwa cisomo cake, anapatsa Abulahamu colowa kudzela m’lonjezo.
19 Tsopano, n’cifukwa ciani Cilamulo cinapelekedwa? Cinapelekedwa kuti macimo aonekele, mpaka mbadwa* imene inapatsidwa lonjezolo itafika. Ndipo Cilamuloco cinapelekedwa ndi angelo kudzela mwa mkhalapakati. 20 Mkhalapakati amafunika ngati cipangano cili pakati pa anthu awili osati mmodzi. Ndi mmenenso zinalili ndi Mulungu, anali yekha, moti sipanafunikile mkhalapakati. 21 Kodi Cilamulo cikutsutsana ndi malonjezo a Mulungu? M’pang’ono pomwe! Ngati lamulo limene lingapeleke moyo n’limene linapelekedwa, ndiye kuti kukhalanso wolungama kukanatheka kudzela m’cilamulo. 22 Koma Malemba amaonetsa kuti anthu akulamulidwa ndi ucimo kuti lonjezolo limene limakhalapo mwa kukhulupilila Yesu Khristu lipatsidwe kwa amene akumukhulupilila.
23 Komabe, cikhulupililoco cisanafike, cilamulo cinali kutiyang’anila, ndipo tinapelekedwa m’manja mwake kuti citisunge. Pa nthawi imeneyo, tinali kuyembekezela cikhulupililo cimene cinali citatsala pang’ono kubvumbulidwa. 24 Conco Cilamulo cinakhala ngati mtsogoleli* wathu wotifikitsa kwa Khristu, kuti tiyesedwe olungama mwa cikhulupililo. 25 Ndiye popeza cikhulupililoco cafika, sitilinso pansi pa wotitsogolela.*
26 Inu nonse ndinu ana a Mulungu cifukwa mumakhulupilila Khristu Yesu. 27 Popeza inu nonse munabatizidwa mwa Khristu, mwabvala Khristu. 28 Motelo, palibe Myuda kapena Mgiriki, kapolo kapena mfulu, mwamuna kapena mkazi, cifukwa nonsenu ndinu amodzi mogwilizana ndi Khristu Yesu. 29 Ndipo, ngati ndinu ake a Khristu, ndiye kuti ndinudi mbadwa* za Abulahamu, olandila colowa malinga ndi lonjezolo.