LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 10
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Paulo akhalila kumbuyo utumiki wake (1-18)

        • Zida zathu za nkhondo si zam’dzikoli (4, 5)

2 Akorinto 10:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2016, masa. 8-9

2 Akorinto 10:5

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    6/2019, masa. 8-13

    Nsanja ya Mlonda,

    8/1/2013, tsa. 27

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 10:1-18

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

10 Tsopano ine Paulo, ndikukudandaulilani mwa kufatsa ndi kukoma mtima kwa Khristu. Ine amene anthu ena amati ndine wofooka ndikamalankhula nanu pamaso m’pamaso, koma wolimba mtima ndikamalankhula nanu ndikakhala kwina. 2 Ndikhulupilila kuti ndikadzafika kumeneko, anthu ena amene akuona kuti ife tinacita zinthu ngati anthu a m’dzikoli adzakhala atasintha kuti ndisadzawadzudzule mwamphamvu. 3 Ngakhale kuti moyo wathu ndi wofanana ndi wa anthu ena onse, sitikumenya nkhondo motsatila maganizo a m’dzikoli. 4 Pakuti zida zathu za nkhondo si zida za m’dzikoli, koma ndi zida zamphamvu zimene Mulungu watipatsa kuti tizigwetsela zinthu zozikika molimba. 5 Pakuti tikugubuduza maganizo komanso cochinga ciliconse cotsutsana ndi kudziwa Mulungu, ndipo tikugonjetsa ganizo lililonse n’kulimanga ngati mkaidi kuti lizimvela Khristu. 6 Komanso ndife okonzeka kupeleka cilango kwa munthu aliyense wosamvela, inu mukaonetsa kuti ndinu omvela pa ciliconse.

7 Mumaona zinthu potengela maonekedwe akunja. Ngati aliyense mumtima mwake amakhulupilila kuti ndi wa Khristu, ndi bwino aziganizilanso mfundo iyi yakuti: Ifenso ndife a Khristu ngati mmene munthuyo alili. 8 Ambuye anatipatsa ulamulilo kuti tikulimbikitseni, osati kukufooketsani. Ndipo ngati ndingadzitamandile mopitililako malile za ulamulilo umenewu, sindingacite manyazi. 9 Pakuti sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga. 10 Popeza ena amati: “Makalata ake amakhala ndi uthenga wamphamvu, koma mwiniwake akakhala pakati pathu amaoneka wofooka, ndipo zokamba zake n’zogwetsa ulesi.” 11 Anthu a maganizo amenewo adziwe kuti zimene tikunena m’makalata athu tili kutali, tidzacitanso zomwezo tikadzabwela. 12 Pakuti sitidziona ngati ndife ofanana ndi anthu amene amadzikweza, ndiponso sitidziyelekezela ndi anthu amenewo. Koma iwo akamayezana okha-okha posewenzetsa mfundo zao n’kumadziyelekezela okha-okha, samvetsa ciliconse.

13 Komabe ife sitidzadzitamandila pa zinthu zimene zili kunja kwa malile amene anatiikila. Koma tidzadzitamandila pa zinthu zimene zili mkati mwa malile a gawo limene Mulungu watipatsa lomwe linafika mpaka kwanuko. 14 Conco sitikudutsa malile a gawo lathu ngati kuti gawolo silifika kwanuko. Pakuti tinali oyamba ndife kufika kwanuko ndi uthenga wabwino wokamba za Khristu. 15 Sikutinso tikudzitamandila pa nchito ya munthu wina imene ili kunja kwa gawo limene anatipatsa. Koma tili ndi cidalilo kuti cikhulupililo canu cikadzaonjezeka, nayonso nchito yathu idzakula m’gawo lathu. Zikatelo tidzakhala ndi zocita zambili, 16 kuti tikalalikile uthenga wabwino ku maiko akutali kupitilila kwanuko, n’colinga cakuti tisadzitamandile pa nchito imene yagwilidwa kale m’gawo la munthu wina. 17 “Koma amene akudzitama, adzitamandile mwa Yehova.” 18 Pakuti munthu amene amabvomelezedwa, si amene amadziyeneleza yekha, koma amene Yehova wamuyeneleza.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani