LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 9
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Alimbikitsidwa kukhala opatsa (1-15)

        • Mulungu amakonda munthu amene amapeleka mocokela pansi pa mtima (7)

2 Akorinto 9:7

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 55

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, tsa. 196

2 Akorinto 9:11

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 210-212

2 Akorinto 9:12

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 210-213

2 Akorinto 9:13

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 210-212

2 Akorinto 9:14

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 210-212, 216

2 Akorinto 9:15

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yogawila),

    na. 2 2017 tsa. 4

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 9-10

    Nsanja ya Mlonda,

    12/15/2015, tsa. 15

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 210-212

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 9:1-15

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

9 Ponena za utumiki wothandiza oyelawo, m’posafunikila kuti ndicite kukulembelani. 2 Cifukwa ndikudziwa kuti muli ndi mtima wofunitsitsa, ndipo ndikunena zimenezi kwa anthu a ku Makedoniya mocita kunyadila. Ndakhala ndikuwauza kuti abale a ku Akaya akhala okonzeka kwa caka cimodzi tsopano, ndipo kudzipeleka kwanu kwalimbikitsa abale oculuka kumeneko. 3 Koma ndikutumiza abale kuti kukunyadilani kwathu kusapite pacabe pa nkhani imeneyi, koma kuti mukhalebe okonzeka monga momwe ndinanenela. 4 Pakuti ngati ndabwela kumeneko ndi anthu a ku Makedoniya n’kupeza kuti sindinu okonzeka, ifeyo ndi inuyo, tingadzacite manyazi cifukwa tikukudalilani kuti ndinu okonzeka. 5 Conco ndaona kuti ndi bwino kuti ndipemphe abale kuti atsogole kubwela kwa inu ife tisanafike, kuti akuthandizeni kukonzelatu mphatso ija imene munalonjeza kuti mudzaipeleka mowolowa manja. Cotelo mphatsoyo idzakhala yokonzelatu, ndipo mudzaipeleka mowolowa manja, osati mokakamizika.

6 Pa nkhani imeneyi, aliyense amene akubzala moumila adzakololanso zocepa. Ndipo aliyense amene akubzala mowolowa manja adzakololanso zoculuka. 7 Aliyense acite malinga ndi zimene watsimikiza mumtima mwake, osati monyinyilika kapena mokakamizika, cifukwa Mulungu amakonda munthu amene amapeleka mocokela pansi pa mtima.

8 Komanso Mulungu angathe kukuonetsani cisomo cake kuti musasowe zinthu zofunikila pa umoyo wanu, ndiponso kuti mukhale ndi zinthu zambili zokuthandizani kugwila nchito iliyonse yabwino. 9 (Monga mmene Malemba amakambila kuti: “Iye wapeleka mphatso zake mowolowa manja kwa osauka, cilungamo cake cidzakhalapo mpaka muyaya.” 10 Tsopano Mulungu amene amapeleka mbeu mosaumila kwa obzala, komanso cakudya kuti anthu adye, adzakupatsani ndi kuculukitsa mbeu zoti mubzale. Ndipo adzaculukitsanso zokolola zanu za cilungamo.) 11 Pa ciliconse, Mulungu adzakudalitsani kuti mukhale owolowa manja pa zonse, ndipo kudzela m’kuwolowa manja kwanu anthu adzatamanda Mulungu. 12 Cifukwa utumiki wothandiza anthu umenewu, sikuti ukungothandiza oyelawa kuti apeze zimene akufunikila ai, koma ukuthandizanso kuti anthu oculuka aziyamika Mulungu m’mapemphelo ao. 13 Cifukwa ca umboni umene utumiki umenewu ukupeleka, anthuwo akulemekeza Mulungu. Zili conco cifukwa inu mwagonjela uthenga wabwino wokamba za Khristu umene mukuulengeza poyela. Komanso mwawagawila mowolowa manja iwowo ndi anthu onse. 14 Iwo amakupemphelelani mocondelela kwa Mulungu, ndipo amaonetsa kuti amakukondani cifukwa ca cisomo cimene Mulungu wakucitilani.

15 Tikuyamika Mulungu cifukwa ca mphatso yake yaulele yosatheka kuifotokoza.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani