Kwa Agalatiya
5 Khristu anatimasula kuti tikhale ndi ufulu umenewu. Cotelo cilimikani, ndipo musalole kuti mumangidwenso mu joko ya ukapolo.
2 Tamvelani! Ine Paulo, ndikukuuzani kuti ngati mungacite mdulidwe, Khristu sadzakhala waphindu kwa inu. 3 Ndikubwelezanso kuuza munthu aliyense amene akucita mdulidwe kuti afunikanso kutsatila zonse za m’Cilamulo. 4 Inu amene mukufuna kuyesedwa olungama mwa cilamulo, mwadzilekanitsa ndi Khristu. Komanso mwatayana ndi cisomo cake. 5 Kunena za ife, kudzela mwa mzimu, tikuyembekezela mwacidwi cilungamo colonjezedwa cimene cimabwela mwa cikhulupililo. 6 Pakuti mwa Khristu Yesu, kudulidwa kapena kusadulidwa kulibe phindu. Koma cofunika ndi cikhulupililo cimene cimaonekela kudzela m’cikondi.
7 Inu munali kuthamanga bwino-bwino. Ndani anakuletsani kuti musiye kumvela coonadi? 8 Kukopeka kwanuku sikukucokela kwa amene anakuitanani. 9 Yisiti* wocepa amafufumitsa mtanda wonse. 10 Ndili ndi cidalilo kuti inu amene muli mu mgwilizano ndi Ambuye, simudzasintha maganizo. Koma amene akukubvutitsaniyo, kaya akhale ndani, adzalandila ciweluzo comuyenelela. 11 Koma kunena za ine abale, ngati ndikulalikilabe kuti anthu azidulidwa, n’cifukwa ciani ndikuzunzidwabe? Zikanakhala conco, ndiye kuti mtengo wozunzikilapo sukanakhalanso copunthwitsa kwa anthu. 12 Ndikanakonda kuti amuna amene akukubvutaniwo, akanangodzifula okha.
13 Abale, munaitanidwa kuti mukhale aufulu. Koma musagwilitse nchito ufulu umenewu ngati mpata wotsatila zilakolako za thupi. Koma tumikilanani mwacikondi monga akapolo. 14 Pakuti Cilamulo conse cagona* pa lamulo limodzi lakuti:* “Uzikonda mnzako mmene umadzikondela wekha.” 15 Koma ngati mupitiliza kulumana ndi kukhadzulana nokha-nokha, samalani kuti mungaonongane.
16 M’malomwake, ndikuti pitilizani kuyenda ndi mzimu, ndipo simudzacita zolakalaka za thupi ngakhale pang’ono. 17 Pakuti zimene thupi limalakalaka zimalimbana ndi mzimu, ndipo naonso mzimu umalimbana ndi thupi. Ziwilizi zimatsutsana kuti musacite zinthu zimene mufuna kucita. 18 Ndiponso ngati mukutsogoleledwa ndi mzimu, simuli pansi pa cilamulo.
19 Tsopano nchito za thupi zimaonekela, ndizo ciwelewele,* zinthu zodetsa, khalidwe lotayilila,* 20 kupembedza mafano, za mizimu, cidani, ndeu, nsanje, kupsya mtima, mikangano, magawano, magulu ampatuko, 21 kaduka, kumwa mwaucidakwa, maphwando oipa,* ndi zina zotelo. Ponena za zinthu zimenezi, ndikukucenjezelanitu monga ndinacitila poyamba paja, kuti amene amacita zimenezi sadzalowa mu Ufumu wa Mulungu.
22 Koma makhalidwe amene mzimu* woyela umabala mwa anthu ndi cikondi, cimwemwe, mtendele, kuleza mtima, kukoma mtima, ubwino, cikhulupililo, 23 kufatsa, ndi kudziletsa. Palibe lamulo loletsa makhalidwe amenewa. 24 Komanso anthu amene ndi ake a Khristu Yesu, anakhomelela pamtengo thupi lao pamodzi ndi zikhumbo zake komanso zilakolako zake.
25 Ngati mzimu ukutitsogolela, tiyeni tipitilize kuyenda molongosoka mwa mzimuwo. 26 Tisakhale odzikuza, oyambitsa mpikisano pakati pathu komanso ocitilana kaduka.