LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 12
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Masomphenya a Paulo (1-7a)

      • “Munga m’thupi” la Paulo (7b-10)

      • Paulo si wotsika pomuyelekezela ndi atumwi apamwamba (11-13)

      • Paulo adela nkhawa Akorinto (14-21)

2 Akorinto 12:1

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, tsa. 8

2 Akorinto 12:2

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, tsa. 8

2 Akorinto 12:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    12/2018, tsa. 8

    Nsanja ya Mlonda,

    7/15/2015, masa. 8-9

2 Akorinto 12:7

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    11/2019, tsa. 9

    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu Kabuku ka Misonkhano,

    5/2019, tsa. 4

    Nsanja ya Mlonda,

    4/1/2014, tsa. 5

2 Akorinto 12:8

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    11/2019, tsa. 9

    Nsanja ya Mlonda,

    4/1/2014, tsa. 5

2 Akorinto 12:9

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    7/2020, masa. 14-19

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    11/2019, tsa. 9

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/2018, tsa. 9

2 Akorinto 12:10

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    7/2020, masa. 14-19

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/2018, tsa. 9

2 Akorinto 12:21

Mawu amunsi

  • *

    M’Cigiriki, por·neiʹa. Onani Matanthauzo a Mau Ena.

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 12:1-21

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

12 Ndiyenela kudzitama ndithu. N’zoona kuti kudzitama kulibe phindu, koma lekani ndilankhule nkhani yokhudza masomphenya ndi mabvumbulutso ocokela kwa Ambuye. 2 Ndikudziwa munthu wina wogwilizana ndi Khristu. Zaka 14 zapitazo, munthuyu anatengedwa ndi kupita naye kumwamba kwacitatu. Kaya anatengedwa ali ndi thupi lake lenileni kapena ai, sindikudziwa. Akudziwa ndi Mulungu. 3 Ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati anatengedwa ali ndi thupi lake lenileni kapena ai, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 4 Munthuyo anatengedwa n’kupita naye m’paradaiso, ndipo anamva mau amene munthu sangawachule komanso n’kosaloleka kuwakamba. 5 Ndidzadzitamandila ponena za munthu ameneyo, koma ponena za ine mwini, sindidzadzitama kupatulapo pa zofooka zanga zokha. 6 Pakuti ngakhale nditafuna kudzitama, sindidzakhala wopanda nzelu cifukwa ndidzanena coonadi. Koma ndimapewa kutelo cifukwa sindikufuna kuti wina anditamande kwambili kuposa pa zimene akuona mwa ine, kapena kumva kwa ine, 7 cabe cifukwa ca mabvumbulutso apadela amene ndinalandila.

Koma kuti ndisamadzikweze mopitilila muyeso, ndinaikidwa munga m’thupi mwanga umene umandilasa. Mungawo ndi mngelo wa Satana amene amandimenya nthawi zonse kuti ndisamadzikweze mopitilila muyeso. 8 Katatu konse ndinapempha Ambuye mocondelela kuti mungawu undicokele. 9 Koma anandiuza kuti: “Cisomo canga cimene ndakuonetsa n’cokukwanila, cifukwa mphamvu zanga zimaonekela bwino kwambili iweyo ukakhala wofooka.” Conco ndidzadzitamandila mokondwela pa zofooka zanga, kuti mphamvu za Khristu zikhalebe pamutu panga ngati tenti. 10 Ndipo cifukwa ca Khristu ndimakondwela ndikakhala wofooka, ndikamanyozedwa, ndikamasowa zofunikila pa umoyo, ndikamazunzidwa, komanso pa zobvuta zina cifukwa ca Khristu. Pakuti ndikakhala wofooka, m’pamene ndimakhala ndi mphamvu.

11 Apa tsopano ndakhala munthu wopanda nzelu. Inu ndi amene mwandikakamiza kutelo. Paja ndinu munafunikila kundiyamikila pa zabwino zimene ndacita. Pakuti si ndine wotsika mwa njila iliyonse poyelekeza ndi atumwi anu apamwambawo, ngakhale kuti mumandiona kuti si ndine kanthu. 12 Kunena zoona, inu munaona umboni wakuti ndine mtumwi. Munaonanso kuti ndinapilila kwambili, ndinacita zizindikilo, zinthu zodabwitsa, komanso nchito zamphamvu. 13 Kodi n’ciani cimene ndinacitila mipingo ina inu osakucitilani, kupatulapo cokhaco cakuti sindinakhale mtolo kwa inu? Conde mundikhululukile pa colakwaci.

14 Aka ndi kacitatu ine kukhala wokonzeka kubwela kwa inu. Ndipo sindidzakhala katundu wolemetsa cifukwa sindikufuna zinthu zanu, koma inuyo. Pakuti si udindo wa ana kusungila makolo ao cuma, koma ndi udindo wa makolo kusungila ana ao cuma. 15 Koma ine ndidzagwilitsa nchito zinthu zanga zonse, ndidzadzipeleka ndi moyo wanga wonse cifukwa ca inu, ndipo ndidzacita zimenezi mosangalala. Conco ngati ine ndimakukondani kwambili conci, kodi inu muyenela kundikonda pang’ono? 16 Koma mulimonsemo, sindinakulemetseni. Komabe inu mumakamba kuti “ndinakupusitsani” komanso “ndinakucenjelelani.” 17 Ndipo inunso mukudziwa kuti sindinakudyeleni masuku pamutu kudzela mwa wina aliyense amene tinamutumiza kwa inu. Ndinatelo ngati? 18 Ndinalimbikitsa Tito kuti abwele kwanuko, ndipo ndinamutumiza limodzi ndi m’bale wina. Tito sanakudyeleni masuku pamutu, anatelo ngati? Iye ndi ine tinaonetsa mzimu umodzi-modzi, ndipo tinacita zinthu mofanana, si conco?

19 Kodi nthawi yonseyi mwakhala mukuganiza kuti tikudzichinjiliza pamaso panu? Dziwani kuti zimene tikunenazi, tikuzinena pamaso pa Mulungu mogwilizana ndi Khristu. Koma okondedwa, ciliconse cimene timacita, timatelo kuti tikulimbikitseni. 20 Ndikuopa kuti mwina ndikadzafika sindidzakupezani mmene ndikufunila. Komanso kuti mwina inenso, sindidzakhala mmene mukufunila. M’malomwake, ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupsyelana mtima, magawano, misece, manong’onong’o, kudzitukumula cifukwa ca kunyada, komanso cipwilikiti. 21 Mwina ndikadzabwelanso, Mulungu wanga angadzandicititse manyazi pamaso panu. Ndipo mwina ndidzalila cifukwa ca anthu ambili amene anacimwa koma sanalape pa khalidwe lao lonyansa la ciwelewele,* ndiponso khalidwe lao lopanda manyanzi limene akhala akucita.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani