Kwa Agalatiya
4 Tsopano zimene ndikufuna kunena ndi izi, malinga ngati wolandila colowa akali mwana, sipakhala kusiyana pakati pa iye ndi kapolo, ngakhale kuti mwanayo ndiye mwini zonse. 2 Koma amakhalabe pansi pa omulela komanso akapitawo oyang’anila cuma cake mpaka tsiku limene atate ake anaikilatu. 3 Mofananamo, nafenso pamene tinali ana, tinali akapolo cifukwa tinali kuyendela mfundo zimene anthu a m’dzikoli amayendela. 4 Koma nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake amene anadzabadwa kwa mkazi, ndipo anakhala pansi pa cilamulo. 5 Anatelo kuti aombole amene anali pansi pa cilamulo n’colinga cakuti Mulungu atitenge n’kukhala ana ake.
6 Tsopano pakuti ndinu ana ake, Mulungu watumiza mzimu wa Mwana wake m’mitima yathu, ndipo umafuula kuti: “Abba,* Atate!” 7 Conco, sindiwenso kapolo koma mwana. Ndipo ngati ndiwe mwana, ndiye kuti ndiwenso wolandila colowa cimene Mulungu adzakupatse.
8 Ngakhale n’telo, pamene simunali kudziwa Mulungu, munali akapolo a zinthu zimene kwenikweni si milungu. 9 Koma tsopano popeza mwadziwa Mulungu, kapena ndinene kuti mwadziwidwa ndi Mulungu, mukubwelelanso bwanji ku mfundo za m’dzikoli zomwe ndi zosathandiza ndiponso zopanda pake, n’kumafunanso kukhala akapolo ake? 10 Mukusunga masiku, miyezi, nyengo, ndi zaka mosamala kwambili. 11 Ndikuda nkhawa kuti mwina, khama langa pa inu langopita pacabe.
12 Abale, ndikukucondelelani kuti mukhale mmene ndilili, cifukwa inenso ndinali monga inu. Koma dziwani kuti simunandilakwile ciliconse. 13 Inu mukudziwa bwino kuti kudwala kwanga n’kumene kunandipatsa mwai woti ndilengeze uthenga wabwino nthawi yoyamba kwa inu. 14 Ngakhale kuti matenda anga anali mayeso kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane.* Koma munandilandila ngati mngelo wa Mulungu komanso ngati Khristu Yesu. 15 Kodi cimwemwe canu capoyamba paja cinapita kuti? Pakuti ndikucitila umboni kuti zikanakhala zotheka, mukanakolowola maso anu n’kundipatsa. 16 Kodi tsopano ndakhala mdani wanu, cabe cifukwa ndakuuzani zoona? 17 Iwo akuyesetsa mwakhama kuti akukopeni, kuti muziwatsatila, koma osati ndi colinga cabwino. Iwo akufuna kukucotsani kwa ine, kuti mukhale ofunitsitsa kuwatsatila. 18 Komabe ndi bwino kuti munthu nthawi zonse azicita khama pokuonetsani cidwi ali ndi colinga cabwino, osati pokhapo ndikakhala nanu. 19 Inu ana anga, tsopano ndikumvanso zowawa ngati za pobeleka mpaka pamene Khristu adzapangike mwa inu. 20 Ndikanakonda ndikanakhala nanu limodzi tsopano kuti ndilankhule nanu mwa njila ina, cifukwa ndathedwa nanu nzelu.
21 Ndiuzeni, inu amene mukufuna kukhala pansi pa cilamulo, kodi simukumva zimene Cilamuloco cikunena? 22 Mwacitsanzo, Malemba amati Abulahamu anali ndi ana aamuna awili, wina kwa wanchito wake wamkazi, ndipo wina kwa mkazi amene anali mfulu. 23 Koma amene anabadwa kwa wanchito wamkaziyo anabadwa mmene ana onse amabadwila, pomwe mwana winayo wobadwa kwa mkazi amene anali mfulu, anabadwa mwa lonjezo. 24 Nkhani imeneyi ili ndi tanthauzo lophiphilitsa. Azimai awiliwa akuimila zipangano ziwili. Cipangano coyamba ndi ca pa Phili la Sinai cimene cimabeleka ana oti akhale akapolo. Ndipo cipanganoco cikuimila Hagara. 25 Tsopano Hagara akuimila Sinai, phili la ku Arabiya, ndipo akufanana ndi Yerusalemu wa lelolino, pakuti ali mu ukapolo limodzi ndi ana ake. 26 Koma Yerusalemu wokwezeka ndi mfulu, ndipo iye ndi mai wathu.
27 Paja Malemba amati: “Sangalala iwe mkazi wosabeleka, amene sunabelekepo mwana. Pfuula mwacisangalalo mkazi iwe, amene sunamvepo zowawa za pobeleka. Pakuti ana a mkazi wosiyidwa ndi ambili kuposa ana a mkazi amene ali ndi mwamuna.” 28 Tsopano inu abale, ndinu ana a lonjezo monga analili Isaki. 29 Koma monga mmene zinalili kuti mwana wobadwa monga ana onse anayamba kuzunza mwana wobadwa mwa mzimu, ndi mmenenso zilili palipano. 30 Ngakhale n’telo, kodi Malemba amati ciani? “Thamangitsa wanchito wamkazi ndi mwana wake, pakuti mwana wa wanchito wamkaziyo sadzalandila colowa pamodzi ndi mwana wa mkazi amene ndi mfulu.” 31 Conco abale, ife ndife ana a mkazi yemwe ndi mfulu, osati a wanchito wamkazi.