LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 7
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Tidziyeletse mwa kucotsa codetsa ciliconse (1)

      • Paulo ali ndi cimwemwe cifukwa ca Akorinto (2-4)

      • Tito abweletsa lipoti labwino (5-7)

      • Cisoni ca umulungu ndi kulapa (8-16)

2 Akorinto 7:1

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 40

    Galamuka!,

    na. 3 2019 masa. 4-5

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 93-95

2 Akorinto 7:2

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “muzitikonda.”

  • *

    Kapena kuti, “komanso sitinacenjelele munthu aliyense.”

2 Akorinto 7:5

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, masa. 17-18

2 Akorinto 7:11

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “opanda cifukwa; opanda mlandu.”

2 Akorinto 7:16

Mawu amunsi

  • *

    Ma Baibo ena amati, “ndimalimba mtima cifukwa ca inu.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 7:1-16

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

7 Conco okondedwa, popeza anatilonjeza zinthu zimenezi, tiyeni tidziyeletse mwa kucotsa ciliconse codetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyela poopa Mulungu.

2 Tipezeleni malo m’mitima yanu.* Ife sitinalakwile munthu aliyense, sitinaipitse aliyense, komanso sitinadyele masuku pamutu munthu aliyense.* 3 Sindikukamba izi kuti ndikuimbeni mlandu ai. Pakuti ndanena kale kuti inuyo muli m’mitima yathu, kuti tifele limodzi kapena tikhale moyo limodzi. 4 Ndili ndi ufulu waukulu wolankhula kwa inu. Ndipo ndimakunyadilani kwabasi. Ndalimbikitsidwa koposa, ndipo ndikusefukila ndi cimwemwe pa mabvuto onse amene tikukumana nao.

5 Titafika ku Makedoniya sitinapumule koma tinapitiliza kukumana ndi masautso osiyana-siyana, monga anthu kutiukila komanso kudela nkhawa abale. 6 Koma Mulungu amene amalimbikitsa anthu opsyinjika mtima, anatilimbikitsa ndi kufika kwa Tito. 7 Komabe cimene cinatilimbikitsa si kufika kwake kokha ai, koma mmenenso inu munamulimbikitsila. Iye anatibweletselanso uthenga wakuti mukufunitsitsa kundiona, muli ndi cisoni kwambili, ndiponso kuti mukundidela nkhawa. Zimenezi zinandisangalatsanso koposa.

8 Ngakhale kuti ndinakumvetsani cisoni ndi kalata yanga, sindikudziimba mlandu kuti ndinailembelanji. Ngakhale kuti poyamba ndinadziimba mlandu, (ndikuona kuti kalatayo inakumvetsani cisoni, koma kwa kanthawi kocepa). 9 Pano ndikusangalala, osati cifukwa ndinakumvetsani cisoni, koma cifukwa cakuti cisoni canuco cinakuthandizani kulapa. Popeza munamva cisoni ca umulungu, zimene tinalembazo sizinakubvulazeni. 10 Cisoni ca umulungu cimathandiza munthu kulapa kuti apeze cipulumutso, popanda munthuyo kudziimba mlandu. Koma cisoni ca dzikoli cimabweletsa imfa. 11 Taonani cangu cacikulu cimene cisoni canu ca umulungu cabala mwa inu. Cabala mtima wofuna kudziyeletsa, kuipidwa nazo zolakwa, kuopa Mulungu, kufunitsitsa kulapa, kukangalika, komanso kukonza zolakwazo. Mwaonetsadi m’njila iliyonse kuti ndinu oyela* pa nkhani imeneyi. 12 Conco pokulembelani, sindinalembe cifukwa ca amene analakwayo, kapena amene analakwilidwayo ai. Ndinatelo kuti khama lanu lofuna kutimvetsela lionekele pakati panu, pamaso pa Mulungu. 13 Zimenezi zatilimbikitsa kwambili.

Kuonjezela pa kulimbikitsidwa kwathuko, tinakondwela kwambili poona cimwemwe ca Tito, cifukwa nonsenu munamusangulutsa. 14 Ndinamuuzadi kuti ndimakunyadilani, ndipo inu simunandicititse manyazi. Conco zonse zimene tinakuuzani zinali zoona. Nazonso zimene tinauza Tito zakuti timakunyadilani, n’zoona. 15 Ndipo cikondi cake pa inu cimakula kwambili akakumbukila kuti nonsenu munali omvela ndipo munamulandila ndi ulemu waukulu. 16 Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupililani pa zonse.*

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani