LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 5
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Kubvala nyumba ya kumwamba (1-10)

      • Utumiki woyanjanitsa anthu ndi Mulungu (11-21)

        • Colengedwa catsopano (17)

        • Akazembe moimilako Khristu (20)

2 Akorinto 5:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/2020, tsa. 23

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, tsa. 18

2 Akorinto 5:5

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “citsimikizo ca (lonjezo la mphamvu la) zinthu zakutsogolo.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 15-16

2 Akorinto 5:14

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 10-11

2 Akorinto 5:15

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 28

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 10-11

2 Akorinto 5:18

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    2/1/2014, tsa. 20

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 209-210

2 Akorinto 5:20

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, masa. 61-62

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 51-52

2 Akorinto 5:21

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “nsembe ya ucimo.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 5:1-21

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

5 Tikudziwa kuti nyumba yathu ya padziko lapansi kapena kuti tenti ino ikadzapasuka, tidzakhala ndi nyumba yocokela kwa Mulungu. Nyumba imeneyo siidzakhala yomangidwa ndi manja, koma yamuyaya ndipo idzakhala kumwamba. 2 M’nyumba imene tikukhalamoyi timabuula, ndipo tikufunitsitsa kubvala nyumba yathu ya kumwamba, 3 kuti tikadzaibvala nyumbayo, tisakapezeke amalisece. 4 Ndipo ife amene tili mu tenti iyi timabuula komanso kulemedwa, cifukwa sitikufuna kuibvula ai, koma tikufuna kubvala nyumba inayo, kuti thupi limene lingafeli, lilowedwe m’malo ndi moyo. 5 Amene anatikonzekeletsa zinthu zimenezi ndi Mulungu, ndipo ndi amenenso anatipatsa mzimu monga cikole ca zinthu zakutsogolo.*

6 Conco timalimba mtima nthawi zonse, ndipo tikudziwa kuti malinga ngati nyumba yathu ili m’thupi, timakhala kutali ndi Ambuye. 7 Cifukwa tikuyenda mwa cikhulupililo, osati mwa zooneka ndi maso. 8 Tikulimba mtima ndipo tingakonde kukhala ndi Ambuye m’malo mokhala m’thupili. 9 Conco kaya tikhale pafupi ndi iye kapena tikhale kutali ndi iye, colinga cathu n’cakuti tikhale obvomelezeka kwa iye. 10 Pakuti tonse tiyenela kudzaonekela ku mpando wa Khristu woweluzila milandu, n’colinga cakuti aliyense alandile mphoto yake malinga ndi zimene anacita ali m’thupi, kaya zabwino kapena zoipa.

11 Cotelo, popeza tikudziwa kuti Ambuye ayenela kuopedwa, tikupitiliza kukopa anthu, ndipo Mulungu akudziwa bwino zolinga zathu. Komabe ndikhulupilila kuti inunso cikumbumtima canu cikudziwa bwino zolinga zathu. 12 Sikuti tayambanso kudzicitila tokha umboni kwa inu. Koma tikukupatsani cifukwa codzitamandila pa ife, kuti muthe kuyankha amene amadzitama cifukwa ca maonekedwe akunja, osati zimene zili mumtima. 13 Ngati tinacita ngati ofuntha, tinacita zimenezo kuti tikondweletse Mulungu. Koma ngati maganizo athu ali bwino-bwino, ndi zothandiza kwa inu. 14 Pakuti cikondi cimene Khristu ali naco cimatikakamiza, cifukwa ife tatsimikiza kuti munthu mmodzi anafela anthu onse, cifukwa onse anali atafa kale. 15 Iye anafela anthu onse kuti amene ali moyo asakhale moyo wongodzisangalatsa okha, koma wosangalatsa amene anawafela n’kuukitsidwa.

16 Kuyambila tsopano, sitiona munthu aliyense mwakuthupi. Ngakhale kuti Khristu tinamuonapo mwakuthupi, tsopano sitikumuonanso motelo. 17 Conco, ngati aliyense ndi wogwilizana ndi Khristu, ndiye kuti ndi colengedwa catsopano. Zinthu zakale zinacoka, ndipo pabwela zinthu zatsopano. 18 Koma zinthu zonse zicokela kwa Mulungu, amene anatithandiza kuti tiyanjanenso naye kudzela mwa Khristu, ndipo anatipatsa utumiki wothandiza anthu kuti ayanjanenso ndi Mulungu. 19 Utumiki wake ndi wakuti tilalikile zakuti Mulungu akuyanjanitsa dziko kwa iye kudzela mwa Khristu, moti Mulungu sanawelengele anthuwo zolakwa zao, ndipo watipatsa nchito yolengeza uthenga wothandiza anthu kuyanjananso ndi iye.

20 Cotelo, ndife akazembe moimilako Khristu, monga kuti Mulungu akucondelela anthu kupitila mwa ife. Monga akazembe a Khristu, tikucondelela anthu powauza kuti: “Yanjananinso ndi Mulungu.” 21 Munthu amene anali wopanda ucimoyo, Mulungu anamusandutsa kukhala ucimo* cifukwa ca ife, kuti kudzela mwa iye, Mulungu ayambe kutiona kuti ndife olungama.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani