LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 1
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Moni (1-3)

      • Paulo ayamika Mulungu cifukwa ca Akhristu a ku Korinto (4-9)

      • Awalimbikitsa kukhala ogwilizana (10-17)

      • Khristu ndi mphamvu komanso nzelu ya Mulungu (18-25)

      • Kudzitama mwa Yehova (26-31)

1 Akorinto 1:12

Mawu amunsi

  • *

    Wochedwanso Petulo.

1 Akorinto 1:13

Mawu amunsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 1:17

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “kulankhula mocenjela.”

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 1:18

Mawu amunsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 1:19

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Ndidzakankhila kumbali.”

1 Akorinto 1:20

Mawu amunsi

  • *

    Kutanthauza katswili wa Cilamulo.

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 1:23

Mawu amunsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 1:24

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/15/2015, masa. 3-7

1 Akorinto 1:27

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, tsa. 18

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 1:1-31

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

1 Ine Paulo, woitanidwa kukhala mtumwi wa Khristu Yesu mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu, pamodzi ndi Sositene m’bale wathu, 2 ndikulembela mpingo wa Mulungu umene uli ku Korinto. Inu amene mwayeletsedwa mwa Khristu Yesu, amene mwaitanidwa kuti mukhale oyela pamodzi ndi onse amene ali kulikonse omwe akuitanila pa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, Ambuye wao komanso Ambuye wathu.

3 Cisomo ndi mtendele wocokela kwa Mulungu Atate wathu ndi Yesu Khristu Ambuye wathu zikhale nanu.

4 Nthawi zonse ndimathokoza Mulungu wanga cifukwa ca inu, poona cisomo ca Mulungu cimene anakucitilani kudzela mwa Khristu Yesu. 5 Ndinu wolemela m’zinthu zonse cifukwa cogwilizana naye, ndipo wakuthandizani kukhala ndi luso la kulankhula komanso kudziwa zinthu zonse, 6 cifukwa umboni wonena za Khristu wakhazikika pakati panu. 7 Palibe mphatso imene mukupelewela pamene muyembekezela mwacidwi kubvumbulutsidwa kwa Ambuye wathu Yesu Khristu. 8 Komanso Mulungu adzakulimbitsani mpaka pamapeto, kuti musakhale ndi cifukwa cokunenezani naco m’tsiku la Ambuye wathu Yesu Khristu. 9 Mulungu amene anakuitanani kuti mukhale ogwilizana ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye wathu, ndi wokhulupilika.

10 Tsopano ndikukudandaulilani abale, m’dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti nonse muzikhala ogwilizana m’zokamba zanu, ndipo pakati panu pasakhale magawano, koma mukhale ogwilizana kwambili pokhala ndi mtima umodzi ndi maganizo amodzi. 11 Cifukwa ena a m’banja la Kuloe andiuza za inu, abale anga, kuti pakati panu pali magawano. 12 Ndikutanthauza kuti ena pakati panu amanena kuti: “Ine ndine wa Paulo,” ena amati, “Ine ndine wa Apolo,” enanso amati, “Ine ndine wa Kefa,”* pamene ena amati, “Ine ndine wa Khristu.” 13 Kodi Khristu ndi wogawikana? Kodi Paulo anapacikidwa pamtengo wozunzikilapo* kuti inu mupulumutsidwe? Kapena kodi munabatizidwa m’dzina la Paulo? 14 Ndikuthokoza Mulungu kuti sindinabatize aliyense wa inu kupatulapo Kirisipo ndi Gayo, 15 moti palibe wina anganene kuti anabatizidwa m’dzina langa. 16 N’zoona kuti ndinabatizanso anthu a m’banja la Sitefana. Koma za enawo, sindikumbukila ngati ndinabatizapo aliyense. 17 Pakuti Khristu sananditume kuti ndizibatiza anthu, koma kuti ndizilengeza uthenga wabwino, osati mwa luso la kulankhula,* kuopela kuti mtengo wozunzikilapo* wa Khristu ungakhale wopanda nchito.

18 Nkhani yokhudza mtengo wozunzikilapowo* ndi cinthu copusa kwa amene akupita ku cionongeko. Koma kwa ife amene tikupulumutsidwa, imeneyi ndi mphamvu ya Mulungu. 19 Pakuti Malemba amati: “Ndidzathetsa nzelu za anthu anzelu, ndipo ndidzakana* kucenjela kwa anthu anzelu.” 20 Kodi munthu wanzelu ali kuti? Mlembi* ali kuti? Katswili wa mtsutso wa nthawi* ino ali kuti? Kodi Mulungu sanapange nzelu za dzikoli kukhala zopusa? 21 Pakuti mwa nzelu zake, Mulungu sanalole kuti anthu a dzikoli agwilitse nchito nzelu zao pomudziwa. M’malomwake, Mulungu anaona kuti ndi bwino kupulumutsa anthu okhulupilila kupitila mu uthenga umene anthu ena amauona kuti ndi wopusa.

22 Ayuda amafuna kuona zizindikilo ndipo Agiriki amafuna-funa nzelu. 23 Koma ife timalalikila za Khristu amene anaphedwa pamtengo wozunzikilapo.* Kwa Ayuda izi n’zopunthwitsa ndipo kwa anthu amitundu ina n’zopusa. 24 Ngakhale n’conco, Ayuda ndi Agiriki amene anaitanidwa, amaona kuti Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndiponso nzelu ya Mulungu. 25 Cifukwa cinthu ca Mulungu cimene anthu amaciona kuti n’copusa, n’canzelu kuposa anthu. Ndipo cinthu ca Mulungu cimene anthu amaciona kuti n’cofooka, n’camphamvu kuposa anthu.

26 Mukuona abale mmene anakuitanilani, kuti si ambili amene anthu akuwaona kuti ndi anzelu amene anaitanidwa, si ambili amphamvu amene anaitanidwa, si ambili a m’mabanja olemekezeka amene anaitanidwa. 27 Koma Mulungu anasankha zopusa za dziko kuti acititse manyazi anthu anzelu, ndipo Mulungu anasankha zinthu zofooka za dziko kuti acititse manyazi zinthu zamphamvu. 28 Mulungu anasankhanso zinthu zonyozeka za dzikoli, komanso zinthu zimene anthu amaziona ngati zopanda pake, zinthu zimene palibe, kuti acititse zinthu zimene zilipo kukhala zopanda mphamvu, 29 n’colinga coti pasapezeke munthu wodzitama pamaso pa Mulungu. 30 Koma inu ndinu wogwilizana ndi Khristu Yesu cifukwa ca Mulunguyo. Yesu ameneyo amationetsa nzelu za Mulungu komanso cilungamo ca Mulungu. Kudzela mwa iye, anthu akhoza kuyeletsedwa, ndipo kudzela mu dipo limenelo, akhoza kumasulidwa, 31 kuti pakhale kugwilizana ndi mmene Malemba amanenela kuti: “Amene akudzitama, adzitame mwa Yehova.”

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani