LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 28
  • Mmene Kamwana, Ka Mose, Kanapulumukila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Kamwana, Ka Mose, Kanapulumukila
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Mose Anasankha Kulambila Yehova
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Cimene Mose Anathaŵila
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 28

Nkhani 28

Mmene Kamwana, Ka Mose, Kanapulumukila

KODI wakaona kamwana kamene kalila, ndipo kagwililila cala, kapena kuti cikumo ca mai uyu? Kamwana kameneka ni ka Mose. Kodi wamudziŵa mtsikana wokongola uyu? Ni mwana wa mfumu Farao.

Mai wake anamubisa Mose kufikila pamene anakwanitsa miyezi itatu, cifukwa sanafune kuti Aiguputo amuphe. Koma cifukwa anali kudziŵa kuti Aiguputo angamupeze, anamubisa kuti amupulumutse.

Mai wa Mose anatenga basiketi ndi kuikonza bwino-bwino kuti madzi asaloŵemo. Ndiyeno anaika ka Mose mu basiketi ndi kuibisa pamaudzu atali m’mbali mwa mtsinje wa Nailo. Miriamu, mlongosi wa Mose, anauzidwa kuti aime capafupi kuti aziona zimene zingacitike kwa kamwanako.

Patapita kanthawi, mwana mkazi wa Farao anafika kumtsinje wa Nailo kuti asambe. Mwadzidzidzi, anaona basiketi pamaudzu atali. Anaitana mmodzi wa atsikana ake omutumikila, ndi kumuuza kuti: ‘Nibweletsele basiketi iyo.’ Pamene mwana wa Farao anatsegula basiketi, anapezamo kamwana kokongola kwambili. Kamwanako kanali kulila, ndipo mwana wa Farao anakamvelela cifundo. Sanafune kuti kamwana aka kaphedwe.

Ndiyeno Miriamu anafika pamene io anali. Ni uyu ali pacithunzi-thunzi apa. Miriamu anafunsa mwana wa Farao kuti: ‘Kodi mufuna kuti nikuitanileni mkazi waciisiraeli kuti akuleleleni mwana uyu?’

Mwana wa Farao anati: ‘Inde cita zimenezo.’

Mwamsanga Miriamu anathamanga kukauza amai ake. Pamene amai a Mose anafika kwa mwana wa Farao, iye anawauza kuti: ‘Tenga mwana uyu ukanilelele, ndipo ine nizikulipila.’

Conco, mai wa Mose anali kusamalila mwana wake-wake. Pamene Mose anakula, mai wake anamubweza kwa mwana wa Farao. Ndipo iye anamutenga kukhala mwana wake. Umu ndi mmene zinacitikila kuti Mose akulile mu nyumba ya Farao.

Ekisodo 2:1-10.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani