LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • fg phunzilo 1 Mafunso. 1-3
  • Kodi Uthenga Wabwino n’Ciani?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Uthenga Wabwino n’Ciani?
  • Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Mulungu Ali Nalo Colinga Canji Dziko Lapansi?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kuyankha Mafunso A m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Mulungu Adzacita Ciani Kutsogolo?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2019
  • Kodi Mulungu Ndani?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
fg phunzilo 1 Mafunso. 1-3

PHUNZILO 1

Kodi Uthenga Wabwino n’Ciani?

1. Kodi uthenga wocokela kwa Mulungu ndi wotani?

Anthu asangalala ndi moyo padziko

Mulungu afuna kuti anthu asangalale ndi umoyo padziko lapansi. Iye analenga dziko lapansi ndi zonse zili mmenemo cifukwa cakuti amakonda anthu. Posacedwapa, adzacitapo kanthu kuti abweletse tsogolo labwino kwa anthu onse. Iye adzapulumutsa mtundu wa anthu ku mavuto onse.—Ŵelengani Yeremiya 29:11.

Palibe boma limene linakwanitsapo kuthetsa ciwawa, matenda, kapena imfa. Koma uthenga wabwino ndi wakuti, posacedwapa, boma la Mulungu lidzaloŵa m’malo mwa maboma onse a anthu. Nzika zake zidzakhala ndi thanzi labwino ndipo zidzakhala pamtendele.—Ŵelengani Yesaya 25:8; 33:24; Danieli 2:44.

2. N’cifukwa ciani uthenga wabwino uli wofunika kwambili?

Mavuto adzatha kokha pamene Mulungu adzacotsa anthu oipa padziko lapansi. (Zefaniya 2:3) Kodi zimenezi zidzacitika liti? Mau a Mulungu anakambilatu za mavuto amene angaononge mtundu wa anthu. Zinthu zoipa zimene zicitika pa dziko lapansi zimaonetsa kuti nthawi yakuti Mulungu acitepo kanthu ili pafupi kwambili.—Ŵelengani 2 Timoteyo 3:1-5.

3. Kodi tiyenela kucita ciani?

Tiyenela kuphunzila za Mulungu m’Mau ake, Baibo. Ili ngati kalata imene atate acikondi atilembela. Imatiuza mmene tingakhalile ndi umoyo wabwino panthawi ino, ndi mmene tingakhalile ndi moyo wosatha mtsogolo pa dziko lapansi. N’zoona kuti anzanu ena sangakonde kuti anthu ena azikuthandizani kumvetsetsa Baibo. Koma popeza kuti Mulungu watilonjeza tsogolo labwino, musalole kuti anthu ena akulepheletseni kuphunzila Baibo.—Ŵelengani Miyambo 29:25; Chivumbulutso 14:6, 7.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani