LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w13 8/1 tsa. 16
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Yandikilani kwa Mulungu Kupitila M’pemphelo
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Mwayi Wa Pemphelo
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Kodi Mungamuyandikile Bwanji Mulungu?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Mawu Oyamba
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
w13 8/1 tsa. 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBO

Kodi Mulungu amamva mapemphelo onse?

Anthu a mitundu yonse akamapemphela, Mulungu amamva. (Salimo 145:18, 19) Mau ake, Baibo, amatilimbikitsa kuti tiyenela kumuuza nkhani iliyonse imene imatidetsa nkhawa. (Afilipi 4:6, 7) Komabe, Mulungu sasangalala ndi mapemphelo ena. Mwacitsanzo, iye sasangalala ndi mapemphelo obweleza-bweleza ndi oloweza pamtima.—Ŵelengani Mateyu 6:7.

Ndiponso Yehova sakondwela ndi mapemphelo a anthu amene amanyalanyaza malamulo ake mwadala. (Miyambo 28:9) Mwacitsanzo, m’nthawi za Baibo, Mulungu anakana kumvela mapemphelo a Aisiraeli amene anali ndi mlandu wakupha anthu. Zimenezi zionetsa bwino kuti pali zinthu zina zimene tiyenela kucita kuti Mulungu amve mapemphelo athu.—Ŵelengani Yesaya 1:15.

Kodi tiyenela kucita ciani kuti Mulungu amve mapemphelo athu?

N’zosatheka kufikila Mulungu m’pemphelo ngati tilibe cikhulupililo. (Yakobo 1:5, 6) Tiyenela kukhulupilila kuti iye aliko ndipo amasamala za ife. Tingalimbitse cikhulupililo cathu mwa kuphunzila Baibo. Tikutelo cifukwa cakuti munthu amafunika kukhala ndi umboni wotsimikizilika wocokela m’Mau a Mulungu kuti akhale ndi cikhululupililo ceni-ceni.—Ŵelengani Aheberi 11:1, 6.

Tiyenela kupemphela mocokela pansi pa mtima ndi modzicepetsa. Ngakhale Mwana wa Mulungu, Yesu, anali kudzicepetsa popemphela. (Luka 22:41, 42) Conco, m’malo mouza Mulungu zocita, tiyenela kuyesetsa kumvetsetsa zimene iye amafuna mwa kuphunzila Baibo. Mwakutelo tidzapemphela mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu.—Ŵelengani 1 Yohane 5:14.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 17 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani