LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 February tsa. 6
  • Kondwelani mu Ciyembekezo Canu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kondwelani mu Ciyembekezo Canu
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Pitilizani Kulimbitsa Ciyembekezo Canu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Kodi Ciyembekezo Codalilika Mungacipeze Kuti?
    Galamuka!—2004
  • Ciyembekezo Cathu N’cosagwilitsa Mwala
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Zifukwa Zokhalila na Ciyembekezo mu 2023—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 February tsa. 6
Banja likonzekela citsanzo ca ulaliki pa Kulambila Kwa Pabanja

UMOYO WACIKHRISTU

Kondwelani mu Ciyembekezo Canu

Ciyembekezo cili ngati nangula. (Aheb. 6:19) Cimatithandiza kuti cikhulupililo cathu cisawonongeke, ngati mmene ngalawa imawonongekela ndi cimphepo ca mkuntho panyanja. (1 Tim. 1:18, 19) Mphepo zamkuntho zingaphatikizepo kugwilitsidwa mwala, kutaikidwa cuma, matenda amgonagona [osacila msanga], imfa ya wokondedwa, kapena vuto lililonse loopseza cikhulupililo cathu.

Cikhulupililo na ciyembekezo zimatithandidza kuona bwino mphoto yathu yamtsogolo. (2 Akor. 4:16-18; Aheb. 11:13, 26, 27) Conco, kaya ciyembekezo cathu n’ca kumwamba kapena padziko lapansi, tiyenela kucilimilila nthawi zonse mwa kusinkha-sinkha malonjezo ali m’Mau a Mulungu. Ndiyeno pamene mayeselo ativutitsa maganizo, tidzakhalabe acimwemwe.—1 Pet. 1:6, 7.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI KONDWELANI NDI CIYEMBEKEZO, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • N’cifukwa ciani Mose n’citsanzo cabwino cofunika kutengela?

  • Mitu ya mabanja ili na udindo wanji?

  • Ni nkhani ziti zimene mungakambilane pa Kulambila kwa Pabanja lanu?

  • Kodi ciyembekezo cingakuthandizeni bwanji kuyang’anizana ndi mayeselo mwacidalilo?

  • N’ciani cimene imwe muyembekezela mwacidwi m’tsogolo?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani