LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb22 March tsa. 5
  • Njila Zitatu Zoonetsela Kuti Timadalila Yehova

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Njila Zitatu Zoonetsela Kuti Timadalila Yehova
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Nkhani Zofanana
  • Mwayi Wa Pemphelo
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Muyandikileni Mulungu Kupitila m’Pemphelo
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mmene Tingapezele Mphamvu m’Malemba
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
  • Khalani ndi Cikhulupililo Ndipo Muzipanga Zosankha Mwanzelu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
mwb22 March tsa. 5

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Njila Zitatu Zoonetsela Kuti Timadalila Yehova

Davide anagonjetsa Goliyati cifukwa codalila Yehova. (1 Sam. 17:45) Yehova amafuna kuonetsa mphamvu zake pothandiza atumiki ake onse. (2 Mbiri 16:9) Tingaonetse bwanji kuti timadalila thandizo limene Yehova amapeleka m’malo modalila cidziŵitso cimene tili naco na maluso athu? Nazi njila zitatu:

  • Muzipemphela kaŵili-kaŵili. Osangopempha cabe cikhululukilo mukalakwitsa cinacake, koma muzipemphanso mphamvu pamene mwayang’anizana na mayeselo. (Mat. 6:12, 13) Osangopempha dalitso la Yehova pa zisankho zimene mwapanga kale, koma muzipemphanso citsogozo cake na nzelu zake musanapange zisankho.—Yak. 1:5

  • Khalani na cizoloŵezi coŵelenga Baibo na kuiphunzila. Muziŵelenga Baibo tsiku lililonse. (Sal. 1:2) Muzisinkhasinkha zitsanzo za m’Baibo, na kugwilitsila nchito zimene mwaphunzila. (Yak. 1:23-25) Muzikonzekela ulaliki m’malo mongodalila luso lanu. Pindulani mokwanila na misonkhano ya mpingo mwa kukonzekelelatu pasadakhale.

  • Muziyendela limodzi na gulu la Yehova. Dziŵani malangizo atsopano a gulu, ndipo atsatileni mwamsanga. (Num. 9:17) Mvelani akulu pamene akupeleka uphungu na malangizo.—Aheb. 13:17

Apolisi atenga m’bale kuti akamuike m’citolokosi; atolankhani na abale ena akuona.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI PALIBE CIFUKWA COCITILA MANTHA NA CIZUNZO, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

• Ni zinthu ziti zimene abale na alongo anali kuopa?

• Cinawathandiza n’ciani kuthetsa mantha awo?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani