LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 45
  • Aoloka Mtsinje Wa Yorodano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Aoloka Mtsinje Wa Yorodano
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Yehova Asankha Yoswa
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Cigumula Cacikulu
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Yoswa Akhala Mtsogoleli
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 45

Nkhani 45

Aoloka Mtsinje Wa Yorodano

ONA! Aisiraeli aoloka mtsinje wa Yorodano! Nanga madzi ali kuti? Popeza kuti mvula imagwa kwambili nthawi imeneyi, mtsinje unali wodzala, koma tsopano mulibe madzi! Ndipo Aisiraeli ayenda pouma monga mmene zinalili pamene anaoloka Nyanja Yofiila! Nanga madzi onse aja ayenda kuti? Tiye tione.

Pamene nthawi ifika yakuti Aisiraeli aoloke mtsinje wa Yorodano, Yehova alamula Yoswa kuti auze anthu kuti: ‘Ansembe adzanyamula likasa la cipangano ndi kukhala kutsogolo, koma ife tidzawatsatila kumbuyo. Ndipo io akangoponda mapazi ao mu mtsinje wa Yorodano, madzi adzaleka kuyenda.’

Conco ansembe anyamula likasa la cipangano, ndi kukhala kutsogolo kwa anthu. Pamene afika pa Yorodano, ansembe aponda m’madzi. Pamtsinje apa m’patali ndipo madzi ake athamanga kwambili. Koma pamene ansembe apondamo, madzi aleka kuyenda! Zimenezi n’zodabwitsa! Cakumene mtsinje ucokela, Yehova waimitsa madzi kukhala damu. Ndipo posapita nthawi, madzi onse auma mu mtsinje.

Ansembe amene anyamula likasa la cipangano ayenda mpaka pakati pa mtsinje wouma umenewu. Kodi waaona pacithunzi-thunzi apa? Iwo aimilila pamenepo mpaka Aisiraeli onse aoloke mtsinje wa Yorodano pouma.

Pamene onse atsiliza kuoloka, Yehova alamula Yoswa kuti auze amuna amphamvu 12 kuti: ‘Pitani mumtsinje pamene paimilila ansembe amene anyamula likasa la cipangano. Mutenge miyala 12, ndipo muiike kumene mudzagona lelo usiku. Ndiyeno mtsogolo ana anu akakufunsani za miyala imeneyi, mukawauze kuti madzi a mumtsinje wa Yorodano anauma pamene likasa la Yehova la cipangano linali kuoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakukumbutsani za cozizwitsa cimeneci.’ Naye Yoswa atenga miyala ina 12 ndi kuiika pamalo pamene paimilila ansembe mu pamtsinjepo.

Potsilizila pake, Yoswa auza ansembe amene anyamula likasa la cipangano kuti: ‘Cokani mumtsinje wa Yorodano.’ Pamene io angocokamo, madzi ayambanso kuyenda.

Yoswa 3:1-17; 4:1-18.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani