LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 53
  • Lonjezo La Yefita

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Lonjezo La Yefita
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Anakondweletsa Atate Wake ndi Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • Mulungu Amakonda Anthu Okhulupilika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Lonjezo la Yefita
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Yefita Anali Munthu Wauzimu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
Onaninso Zina
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 53

Nkhani 53

Lonjezo La Yefita

KODI unalonjezapo cinthu cimene pambuyo pake cinakuvuta kukwanilitsa? Uyu munthu ali apa anacita zimenezo, ndipo ndiye cifukwa cake alila. Mwamuna ameneyu ni woweluza wolimba mtima wa Aisiraeli, dzina lake ni Yefita.

Yefita akhalako panthawi imene Aisiraeli aleka kulambila Yehova. Iwo acitanso vinthu voipa. Conco Yehova alola Aamoni kuti avutitse Aisiraeli. Zimenezi zicititsa Aisiraeli kulilila kwa Yehova kuti: ‘Takucimwilani. Conde, Tipulumutseni!’

Anthu ali ndi cisoni cifukwa ca zinthu zoipa zimene acita. Iwo aonetsa cisoni cao mwa kuyambanso kulambila Yehova. Ndipo Yehova awathandizanso.

Anthu asankha Yefita kuti awatsogolele pamene adzamenyana ndi Aamoni oipa aja. Yefita afunitsitsa kwambili kuti Yehova amuthandize pocita nkhondo. Conco iye alonjeza Yehova kuti: ‘Ngati n’dzapambana Aamoni pankhondo, n’dzapeleka kwa inu munthu woyamba amene adzatuluka m’nyumba yanga kudzanilandila pocokela kunkhondo.’

Yehova wamvela lonjeza la Yefita, ndipo amuthandiza kupambana nkhondo. Kodi umudziŵa munthu woyamba amene atuluka m’nyumba ya Yefita kuti amulandile pamene iye abwelela kucoka kunkhondo? Ni mwana wake mkazi, ndipo iye ndiye mwana wake mmodzi yekha. Pamene Yefita aona mwana wake, alila kuti: ‘Mama ine mwana wanga! Wanibweletsela cisoni. Nalonjeza Yehova ndipo siningasinthe lonjezo langa.’

Pamene mwana wa Yefita akumva za lonjezo limeneli, naye poyamba amvela cisoni. Cifukwa zimenezi zitanthauza kusiya atate ake ndi anzake, ndi kupita kukatumikila Yehova moyo wake wonse, ku cihema ca Yehova ku Silo. Koma auza atate ake kuti: ‘Ngati mwalonjeza Yehova, citani mogwilizana ndi zimene mwalonjeza.’

Conco mwana wa Yefita apita ku Silo, ndipo atumikila Yehova kwa moyo wake wonse pa cihema ca Yehova. Akazi a mu Isiraeli amapita kukamuona masiku anai caka ciliconse, ndipo asangalala naye capamodzi. Anthu amukonda mwana wa Yefita cifukwa ni mtumiki wabwino wa Yehova.

Oweruza 10:6-18; 11:1-40.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani