LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 115
  • Paladaiso Yatsopano Padziko Lapansi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Paladaiso Yatsopano Padziko Lapansi
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • “Tidzaonana M’Paradaiso!”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Kodi Mulungu Ali Nalo Colinga Canji Dziko Lapansi?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Ufumu Umene Udzalamulila Dziko Lonse
    Phunzitsani Ana Anu
  • “Udzakhala Ndi Ine m’Paradaiso”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
Onaninso Zina
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 115

Nkhani 115

Paladaiso Yatsopano Padziko Lapansi

ONA mitengo itali-itali, maluŵa okongola ndi mapili atali-atali pacithunzi-thunzi apa. Malo awa ni abwino, si conco? Ona mmene ka insa kadyela padzanja la kamnyamata aka. Ndipo ona mikango ndi mahosi amene aimilila apo m’dambo. Kodi sungakonde kukhala pa nyumba imene ili m’malo ngati amenewa?

Mulungu afuna kuti ukakhale ndi moyo wamuyaya m’paladaiso padziko lapansi. Ndipo safuna kuti uzimvela zoŵaŵa zimene anthu amavutika nazo masiku ano. Lonjezo la m’Baibo kwa anthu amene adzakhala m’paladaiso yatsopano n’lakuti: ‘Mulungu adzakhala nao. Sikudzakhala imfa kapena kulila kapena zopweteka. Zinthu zakale zapita.’

Yesu adzatsimikizila kuti kusintha kwabwino kumeneku kwacitika. Kodi adzacita zimenezi liti? Adzacita zimenezi pambuyo pakuti wayeletsa dziko lapansi mwa kucotsapo voipa ndi anthu onse oipa. Kumbukila kuti pamene Yesu anali padziko lapansi anacilitsa anthu amene anali ndi matenda osiyana-siyana, ndipo anaukitsanso ngakhale akufa. Yesu anacita izi kuonetsa zimene adzacita pamene adzakhala Mfumu ya Ufumu wa Mulungu.

Ganiza cabe mmene mudzakhalila mwabwino m’paladaiso yatsopano padziko lapansi! Yesu, pamodzi ndi anthu amene adzasankha, adzalamulila kucokela kumwamba. Mafumu amenewa adzasamalila aliyense padziko lapansi ndi kutsimikiza kuti munthu aliyense ni wokondwela. Tiye tione zimene tiyenela kucita kuti tikhale otsimikiza kuti Mulungu adzatipatsa moyo wamuyaya m’paladaiso yake yatsopano.

Chivumbulutso 21:3, 4; 5:9, 10; 14:1-3.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani