LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • ll gao 9 masa. 20-21
  • Kodi Paladaiso Idzabwela Liti?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Paladaiso Idzabwela Liti?
  • Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
  • Nkhani Zofanana
  • Paladaiso Ili Pafupi!
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Gao 9
    Mvetselani kwa Mulungu
  • Kodi Tili mu “Masiku Otsiliza”?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Mapeto A Dziko Ali Pafupi?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
Onaninso Zina
Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
ll gao 9 masa. 20-21

GAO 9

Kodi Paladaiso Idzabwela Liti?

Mavuto amene ali padziko lapansi aonetsa kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi. Luka 21:10, 11; 2 Timoteyo 3:1-5

Mavuto ofala m’masiku otsiliza—njuga, nkhondo, matenda, njala, kusamvela makolo, ndi nkhanza za panyumba

Zinthu zambili zimene zicitika masiku ano, Baibo inakambilatu kuti zidzacitika. Inakamba kuti anthu adzakhala okonda ndalama, osamvela makolo, oopsa, ndi okonda zosangalatsa.

Kudzakhala zivomezi zazikulu, nkhondo, njala, ndi matenda oculuka. Zinthu zimenezi zikucitika masiku ano.

Wa Mboni za Yehova alalikila uthenga wabwino wa ufumu wa Mulungu kwa munthu wina wake

Yesu anakambanso kuti uthenga wabwino wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi.—Mateyu 24:14.

Ufumu wa Mulungu udzacotsa zoipa zonse. 2 Petulo 3:13

Oipa akuwonongedwa pa Aramagedo, ndiyeno Satana na viŵanda vake akulangidwa

Posacedwa Yehova adzaononga anthu onse oipa.

Satana ndi viŵanda vake adzalangidwa.

Yesu wakhala pa mpando wake wacifumu kumwamba, ndipo anthu a mitundu yosiyana-siyana akukondwela

Amene amamvetsela kwa Mulungu adzapulumuka ndi kukhala m’dziko latsopano lolungama, limene simudzakhalanso mantha, ndipo anthu adzakhulupililana ndi kukondana.

  • Kodi Yesu anakamba kuti kudzacitika ciani masiku ano?—Mateyu 24:3-14.

  • Anthu oipa adzaonongedwa.—2 Petulo 3:7.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani