LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 1 tsa. 8
  • Mulungu Anapanga Kumwamba na Dziko Lapansi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mulungu Anapanga Kumwamba na Dziko Lapansi
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Mulungu Ayamba Kupanga Vinthu
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Munda Wokongola
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Mmene Angelo Angakuthandizileni
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 1 tsa. 8
Munda wa Edeni

PHUNZILO 1

Mulungu Anapanga Kumwamba na Dziko Lapansi

Yehova Mulungu ndiye anatilenga ife. Anapanga zinthu zonse, zimene timaona na zimene sitiona. Akalibe kupanga zinthu zimene timaona, anapanga angelo ambili-mbili. Kodi angelo uwadziŵa? Angelo ndi anthu a mzimu okhala kumwamba, ofanana na Yehova. Nawonso Yehova ndiye anawalenga. Angelo sitingawaone, monga mmene sitingaonele Mulungu. Mngelo woyamba amene Yehova anapanga anakhala mthandizi wake. Mngelo ameneyo anathandiza Yehova kupanga nyenyezi, mapulaneti, na zinthu zina zonse. Imodzi mwa mapulaneti amenewo, ni dziko lapansi, limene ni malo okongola okhalapo.

Ndiyeno, Yehova anakonza bwino dziko lapansi kuti pakhale nyama ndi anthu. Anapanga dzuŵa kuti liziunika pa dziko. Anapanganso mapili, nyanja, na mitsinje.

N’ciani cina cimene anapanga? Yehova anati: ‘Nidzapanga maudzu, zomela, na mitengo.’ Panamela mitengo yolekana-lekana ya zipatso, zakudya zamasamba, na maluŵa osiyana-siyana. Kenako, Yehova anapanga zinyama zonse zouluka, zonyaya, zokwaŵa, komanso zoyendela pamimba. Anapanganso tunyama tung’ono-tung’ono monga tukalulu, komanso vikulu-vikulu monga njovu. Nanga iwe, ni nyama iti imene umakonda ngako?

Ndiyeno, Yehova anauza mngelo woyamba kuti: “Tiyeni tipange munthu.” Anthu anakhala osiyana na vinyama. Iwo anakwanitsa kupanga zinthu, kulankhula, kuseka, na kupemphela. Anali kudzasamalila dziko na vinyama. Kodi umudziŵa munthu amene anali woyamba kulengedwa? Tidzaona m’nkhani yotsatila.

“Pa ciyambi, Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.”—Genesis 1:1

Mafunso: Kodi Yehova Mulungu n’ndani? Nanga Yehova anapanga ciani?

Genesis 1:1-26; Miyambo 8:30, 31; Yeremiya 10:12; Akolose 1:15-17

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani