LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb masa. 72-73
  • Mawu Oyamba a Cigawo 6

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mawu Oyamba a Cigawo 6
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Kucokela Pamene Mulungu Anapulumutsa Aisiraeli ku Iguputo, Kukafika pa Mfumu Yao Yoyamba
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Mulungu Amakonda Anthu Okhulupilika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Anakondweletsa Atate Wake ndi Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • Rute Ndi Naomi
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Onaninso Zina
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb masa. 72-73
Samsoni wanyamula geti ya mzinda wa Gaza

Mawu Oyamba a Cigawo 6

Pamene Aisiraeli anafika ku Dziko Lolonjezedwa, cihema cinakhala likulu lolambililako Yehova m’dzikolo. Ansembe anali kuphunzitsa Cilamulo, ndipo oweluza anali kutsogolela mtundu. Cigawo cino cionetsa mmene zosankha na zocita za munthu zimakhudzila anthu ena. Mwisiraeli aliyense anali na udindo kwa Yehova, komanso kwa munthu mnzake. Onetsani mmene zocita za Debora, Naomi, Yoswa, Hana, mwana wamkazi wa Yefita, na Samueli zinakhudzila anthu ambili. Onetsani kuti ngakhale anthu amene sanali Aisiraeli, monga Rahabi, Rute, Yaeli, komanso Agibeoni, anasankha kukhala kumbali ya Aisiraeli cifukwa anadziŵa kuti Mulungu anali nawo.

MAPHUNZILO AKULU-AKULU M’CIGAWOCI

  • Yehova anagwilitsila nchito oweluza kupulumutsa anthu ake mozizwitsa

  • Anthu okhulupilika, acikulile pamodzi na acicepele, anadalitsidwa cifukwa codalila Yehova na mtima wonse

  • Mulungu alibe tsankho. Amalandila anthu a mitundu yonse komanso zikhalidwe zonse, amene amam’konda na kucita zabwino

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani