CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | YOBU 16-20
Limbikitsani Ena ndi Mau Abwino
Zokamba zathu ziyenela kulimbikitsa ena
16:4, 5
Yobu anali wopsinjika maganizo ndi wothedwa nzelu, cakuti anafuna thandizo ndi cilimbikitso kwa ena
Anzake atatu a Yobu sanakambe mau alionse omulimbikitsa. M’malomwake, anamuimba mlandu ndi kuonjezela nkhawa zake
Mau oipa a Bilidadi anacititsa Yobu kulila mosautsidwa mtima
19:2, 25
Yobu analilila kwa Mulungu kuti amuthandize, ngakhale kum’pempha kuti afe
Yobu anali ndi ciyembekezo cakuti adzaukitsidwa, ndipo anapitiliza kupilila mokhulupilika