LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb16 June tsa. 3
  • Khulupililani Yehova ndi Kucita Zabwino

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Khulupililani Yehova ndi Kucita Zabwino
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Nkhani Zofanana
  • Salimo 37:4—“Udzikondweretsenso mwa Yehova”
    Kufotokoza Mavesi a m’Baibulo
  • N’zotheka Kuti Muziwadalila Abale Anu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Muzikhulupilila Yehova Nthawi Zonse
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • “Khulupilila Yehova Ndipo Cita Zabwino”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
mwb16 June tsa. 3

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | MASALIMO 34-37

Khulupililani Yehova ndi Kucita Zabwino

“Usapse mtima [ndi] . . . anthu ocita zosalungama”

37:1, 2

  • Musaleke kutumikila Yehova cifukwa coona kuti anthu oipa zinthu zikuwayendela bwino. Ikani maganizo anu pa madalitso ndi zolinga za kuuzimu

“Khulupilila Yehova ndipo cita zabwino”

37:3

  • Khulupililani Yehova kuti adzakuthandizani mukakhala ndi nkhawa. Adzakuthandizani kukhalabe wokhulupilika

  • Khalani wotangwanika mwa kuuzako ena za Ufumu wa Mulungu

“Sangalala mwa Yehova”

37:4

  • Pezani nthawi yoŵelenga ndi kusinkhasinkha Mau a Mulungu kuti mum’dziŵe bwino Yehova

“Lola kuti Yehova akutsogolele panjila yako”

37:5, 6

  • Khulupililani kwambili Yehova kuti adzakuthandizani kuthetsa vuto lililonse

  • Pitilizani kukhala ndi khalidwe labwino pamene mutsutsidwa kapena kuzunzidwa

“Khala cete pamaso pa Yehova, ndipo umuyembekezele ndi mtima wako wonse”

37:7-9

  • Pewani kucita zinthu mopupuluma, zimene zingakuonongeleni cimwemwe ndi citetezo canu cauzimu

“Anthu ofatsa adzalandila dziko lapansi”

37:10, 11

  • Khalani ofatsa, ndipo yembekezelani Yehova kuti acotsepo mavuto onse amene mukumana nao

  • Muzithandiza Akristu anzanu ndi kutonthoza amene akuvutika maganizo, mwa kuwauza lonjezo la Mulungu la dziko latsopano, limene lili pafupi kwambili

Mngelo atambasulila manja ake pa dziko lapansi la Paradaiso

Ufumu wa Mesiya udzabweletsa madalitso osaneneka

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani