LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 April tsa. 5
  • Mukhoza Kulimbikitsa Mkhristu Wozilala

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mukhoza Kulimbikitsa Mkhristu Wozilala
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • “Bwelelani kwa Ine”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • “Inetu Ndidzafunafuna Nkhosa Zanga”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 April tsa. 5

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Mukhoza Kulimbikitsa Mkhristu Wozilala

M’busa afuna kupulumutsa nkhosa yosocela

Pa ciŵili, April 11, Akhristu ozilala ambili adzapezeka pa Cikumbutso. Anayamba bwino kuthamanga pa mpikisano wa moyo, koma afooka pa zifukwa zosiyana-siyana. Zifukwa zina azifotokoza m’kabuku kakuti Bwelelani kwa Yehova. (Aheb. 12:1) Ngakhale n’conco, ozilala amenewa ni amtengo wapatali kwa Yehova cifukwa anawagula na magazi a Mwana wake. (Mac. 20:28; 1 Pet. 1:18, 19) Nanga tingawathandize bwanji kuti abwelele ku mpingo?

Akulu a mpingo amasakila anthu ozilala kuti awathandize, monga mmene m’busa amasakilila mwakhama nkhosa zimene zasocela. (Luka 15:4-7) Izi zimaonetsa cikondi na cisamalilo ca Yehova. (Yer. 23:3, 4) Koma si akulu okha, tonse tikhoza kuwalimbikitsa ozilala. Khama lathu poonetsa kukoma mtima na cikondi zimam’kondweletsa Yehova, ndipo zingabweletse mapindu osaneneka. (Miy. 19:17; Mac. 20:35) Conco, ganizilani amene mungam’limbikitse, ndipo teloni mwamsanga.

Laura ayang’ana pawindo, pamene Abbey apemphela, kenako Abbey na Laura akumbatilana

TAMBANI VIDIYO YAKUTI LIMBIKITSANI OZILALA, NDIYENO KAMBILANANI MAFUNSO AYA:

  • N’ciani cimene Abbey anacita atakumana ndi wa Mboni amene sanali kudziŵana naye?

  • N’cifukwa ciani tiyenela kudziŵitsa akulu ngati taganiza zothandiza munthu wozilala?

  • Kodi Abbey anakonzekela bwanji pokacezela Laura kaciŵili?

  • Kodi Abbey anaonetsa bwanji khama, kuleza mtima, na cikondi poyetsa kulimbikitsa Laura?

  • Tingaphunzilenji pa fanizo la Yesu la pa Luka 15:8-10?

  • Ni madalitso anji amene anatsatilapo cifukwa ca khama la Akhristu osiyana-siyana pothandiza Laura?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani