LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 May tsa. 8
  • “Cimene Mulungu Wacimanga Pamodzi . . . ”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Cimene Mulungu Wacimanga Pamodzi . . . ”
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Muzilemekeza “Cimene Mulungu Wacimanga Pamodzi”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Mafunso Ocokela kwa Oŵelenga
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 May tsa. 8
Mwamuna na mkazi agwililana manja

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

“Cimene Mulungu Wacimanga Pamodzi . . . ”

Cilamulo ca Mose cinali kufuna kuti mwamuna amene anali kuganizila zosudzula mkazi wake azilemba kalata yacilekanilo yovomelezeka mwalamulo. Izi zinali kuthandiza kuti anthu asamasudzulane mwacisawawa. Komabe, atsogoleli a cipembedzo a m’nthawi ya Yesu anali kulola anthu kusudzulana mwacisawawa. Amuna anali kusudzula akazi awo pa cifukwa ciliconse. (nwtsty mfundo zounikila pa Maliko 10:4, 11) Yesu anakumbutsa anthu mfundo yakuti Yehova ndiye anayambitsa cikwati. (Maliko 10:2-12) Mwamuna na mkazi afunika kukhala “thupi limodzi” kwa moyo wawo wonse. Pa nkhani imeneyi, Mateyu analemba kuti cifukwa cimodzi cokha ca m’Malemba cothetsela cikwati ni “cigololo.”—Mat. 19:9.

Masiku ano, anthu ambili saona cikwati mmene Yesu anali kucionela. Amacipeputsa monga Afarisi. Anthu a m’dzikoli akakumana na mavuto m’banja, amathamangila kuthetsa cikwati. Koma Akhristu okwatilana amalemekeza kwambili malumbilo awo a cikwati, ndipo amayesetsa kuthetsa mavuto mwa kutsatila mfundo za m’Baibo. Pambuyo potamba vidiyo yakuti; Cikondi na Ulemu Zimagwilizanitsa Banja, yankhani mafunso aya:

  • Aŵelenga Baibo; mwamuna amvetsela pamene mkazi wake akamba; pikica ya cikwati yong’ambika

    Kodi mungaseŵenzetse bwanji mfundo ya pa Miyambo 15:1 m’cikwati canu? Nanga n’cifukwa ciani kucita zimenezo n’kofunika?

  • Kodi kuseŵenzetsa mfundo ya pa Miyambo 19:11 kungakuthandizeni bwanji kupewa mavuto?

  • Ngati cikwati canu cili pa mavuto aakulu, m’malo moganiza kuti, ‘Tingosudzulana cabe,’ mungadzifunse mafunso abwanji?

  • Kodi kuseŵenzetsa mfundo ya pa Mateyu 7:12 kungakuthandizeni bwanji kukhala mwamuna kapena mkazi wabwino?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani