LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 September tsa. 7
  • Kodi Mungapeleke Nthawi na Mphamvu Zanu?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Mungapeleke Nthawi na Mphamvu Zanu?
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Dzipelekeni Kuthandiza pa Nchito Zomanga za Gulu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Nchito Yomanga Inayenda Bwino Mlili Usanayambe
    Mmene Zopeleka Zanu Zimagwilila Nchito
  • Nchito Yomanga Imene Imalemekeza Yehova
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 September tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Kodi Mungapeleke Nthawi na Mphamvu Zanu?

M’bale amwetulila pamene adula nsimbi pa cimango.

Monga mmene Yesaya analosela, gawo la gulu la Yehova la padziko lapansi likukula kuposa na kale lonse. (Yes. 54:2) Conco, pakufunika kumanga Nyumba za Ufumu zatsopano, Mabwalo a Misonkhano, komanso ma Ofesi a Nthambi. Pambuyo pakuti zamangidwa, zimango zimenezi zimafunika kuzisamalila, ndipo m’kupita kwa nthawi zina zimafunika kukonzedwanso. Zimenezi zimatipatsa mwayi wopeleka nthawi na mphamvu zathu kwa Yehova. Motani?

  • Tingacite zimenezi mwa kutengako mbali yoyeletsa pa Nyumba ya Ufumu pamene kagulu kathu ka ulaliki kakuyeletsa

  • Tingadzipeleke kuti ticiteko maphunzilo a mmene tingasamalile Nyumba ya Ufumu

  • Tingadzaze fomu ya Local Design/Construction Volunteer (DC-50) kuti tizithandizilako mwa apo ndi apo pa nchito yomanga na kusamalila zimango zili kufupi na kumene tikhala

  • Tingadzaze fomu yochedwa Application for Volunteer Program (A-19) na kudzipeleka kuti tizithandizila kwa wiki imodzi kapena kuposelapo m’gawo la Nthambi yathu kapena ku Nthambi ina

TAMBANI VIDIYO YAKUTI KUKONZEKELA KUMANGA CIMANGO CATSOPANO—KAMBALI KAKE NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Kodi pakhala cionjezeko cotani pankhani yoseŵenzetsa mavidiyo kungoyambila mu 2014?

  • Kuti tipitilizebe kukhala na mavidiyo pa kulambila kwathu, kodi pakulinganizidwa yanji, ndipo nchitoyo idzatenga utali wotani?

  • Nanga anchito odzipeleka angacilikize bwanji nchitoyo?

  • Ngati tifuna kuthandizako nchito yomanga ya ku Ramapo, n’cifukwa ciani tifunika kusaina fomu ya DC-50 komanso kuthandizila m’Dipatimenti Yoona za Mapulani ndi Zomangamanga (LDC) ya kwanuko?

  • Kodi pali umboni wotani woonetsa kuti Yehova akutsogolela nchito imeneyi?

  • Kodi tingacilikize bwanji nchito imeneyi olo kuti sitingakwanitse kupita kukamanga nawo?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani