LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w20 May masa. 8-11
  • Mafumu Aŵili Olimbana M’nthawi Yamapeto

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mafumu Aŵili Olimbana M’nthawi Yamapeto
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • Nkhani Zofanana
  • “Mfumu ya Kumpoto” M’nthawi Yamapeto
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • Kodi “Mfumu ya Kumpoto” Ndani Masiku Ano?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • Buku la Chivumbulutso—Cimene Cidzacitikila Adani a Mulungu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Phunzilani ku Maulosi a m’Baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
w20 May masa. 8-11

Mafumu Aŵili Olimbana M’nthawi Yamapeto

Maulosi ena m’chati ino akamba zinthu zimene zinacitika panthawi yofanana. Maulosi onsewa amatsimikizila kuti tikukhala ‘m’nthawi yamapeto.’​—Dan. 12:4.

Chati ya maulosi okamba za mfumu ya kumpoto na mfumu ya kum’mwela. Chatiyi ionetsanso maboma amene anali kuimila mafumu aŵiliwa kuyambila mu 1870 mpaka masiku ano.
  • Chati yoyamba pa machati 4, ionetsa maulosi osiyana-siyana ofotokoza za masiku otsiliza ano. Maulosiwa afotokoza zocitika kuyambila m’caka ca 1870 mpaka 1918, ndipo zina mwa zocitikazo zinacitika pa nthawi imodzi. Zaka zoyambila mu 1914 mpaka kutsogolo, zafotokozedwa kukhala masiku otsiliza. Ulosi 1: Cilombo ca mitu 7 cimene cinawonekela kale-kale caka ca 1870 cisanakwane. Mkati mwa Nkhondo Yoyamba Yapadziko Lonse mutu wa 7 wa cilomboci unavulazidwa. Kuyambila mu 1917, mutu wa 7 umenewo unacila, ndipo cilombo cinakhalanso ca mphamvu. Ulosi 2: Mfumu ya kumpoto inaonekelanso mu 1871, ndipo mfumu ya kumwela inaonekelanso mu 1870. Mfumu ya kumpoto inali boma la Germany. Mfumu ya kum’mwela poyamba inali Great Britain. Koma mu 1917, Ulamulilo Wamphamvu Padziko Lonse wa Britain na America ndiwo unakhala mfumu ya kumwela. Ulosi 3: Kuyambila m’zaka za m’ma 1870, M’bale Charles T. Russell na anzake ndiwo anali ‘mthenga.’ Kuciyambi kwa zaka za m’ma 1880, magazini ya Zion’s Watch Tower inalimbikitsa oŵelenga magaziniyi kuti azilalikila uthenga wabwino. Ulosi 4: Kuyambila mu 1914 kupita mtsogolo, nyengo yokolola. Namsongole akumucotsa pakati pa tiligu. Ulosi 5: Kuyambila mu 1917, mapazi acitsulo cosakanizika na dongo anaonekela. Chati ionetsanso izi: Zocitika za padzikoli kuyambila mu 1914 mpaka mu 1918, Nkhondo Yoyamba Yapadziko Lonse. Zocitika zokhudza anthu a Yehova: Kuyambila mu 1914 mpaka 1918, Ophunzila Baibo anaponyedwa m’ndende ku Britain na ku Germany. Mu 1918, abale kulikulu lathu anaponyedwa m’ndende ku America.
    Ulosi 1.

    (Ma)lemba Chiv. 11:7; 12:13, 17; 13:1-8, 12

    Ulosi “Cilombo” cakhala cikulamulila padzikoli kwa zaka zoposa 3,000. M’nthawi ya mapeto, mutu wa 7 wa cilomboco unavulazidwa. Pambuyo pake, mutuwo unacila ndipo “dziko lonse” lapansi linatsatila cilomboco. Satana amaseŵenzetsa cilomboci ‘pocita nkhondo ndi otsala.’

    Kukwanilitsidwa kwake Cigumula citapita, maboma a anthu otsutsana na Yehova anayamba kulamulila padzikoli. Patapita zaka zoposa 3,000, padzikoli panacitika Nkhondo Yoyamba Yapadziko Lonse. Pa nthawi ya nkhondoyo, limodzi mwa maboma amphamvu lochedwa Britain linacepa mphamvu kwambili. Boma la Britain linakhalanso lamphamvu litagwilizana na boma la America. Maka-maka m’nthawi ya mapeto ino, Satana wakhala akuseŵenzetsa maboma onse a anthu pozunza atumiki a Mulungu.

  • Ulosi 2.

    (Ma)lemba Dan. 11:25-45

    Ulosi Kulimbana kwa mfumu ya kumpoto na mfumu ya kum’mwela m’nthawi yamapeto.

    Kukwanilitsidwa kwake Dziko la Germany linacita nkhondo na Britain na America. Mu 1945, boma la Soviet Union na maiko ogwilizana nalo anakhala mfumu ya kumpoto. Mu 1991, boma la Soviet Union linatha, ndipo m’kupita kwa nthawi dziko la Russia na maiko ogwilizana nalo ndiwo anakhala mfumu ya kumpoto.

  •  Ulosi 3.

    (Ma)lemba Yes. 61:1; Mal. 3:1; Luka 4:18

    Ulosi Yehova adzatumiza “mthenga” wake kuti ‘akonze njila’ Ufumu wa Mesiya usanakhazikitsidwe. Mthengayo adzalengeza “uthenga wabwino kwa anthu ofatsa.”

    Kukwanilitsidwa kwake Kuyambila m’ma 1870, M’bale C. T. Russell na anzake anali kuphunzila Baibo mwakhama kuti amvetsetse coonadi na kuuzako ena. M’zaka za m’ma 1880, iwo anayamba kulimbikitsa atumiki a Mulungu kuti azilalikila. Anafalitsa nkhani monga yakuti, “Alaliki 1,000 Akufunika,” komanso yakuti “Anadzozedwa Kuti Azilalikila.”

  •  Ulosi 4.

    (Ma)lemba Mat. 13:24-30, 36-43

    Ulosi Munthu anafesa tiligu m’munda. Mdani anabwela na kufesamo namsongole. Namsongoleyo analoledwa kukula mpaka kuphimba tiligu. Panthawi yokolola, namsongoleyo akumucotsa pakati pa tiligu.

    Kukwanilitsidwa kwake Kuyambila mu 1870, kusiyana pakati pa Akhristu oona na Akhristu onama kunayamba kuonekela kwambili. M’nthawi ya mapeto, Akhristu oona akusonkhanitsidwa na kulekanitsidwa na Akhristu onama.

  •  Ulosi 5.

    (Ma)lemba Dan. 2:31-33, 41-43

    Ulosi Mapazi a fano lopangidwa na zinthu zosiyana-siyana. Mapaziwo ni acitsulo cosakanizika na dongo.

    Kukwanilitsidwa kwake Dongo ni anthu wamba olamulidwa na Britain na America amene amatsutsa maboma amenewa. Anthu amenewa amapangitsa kuti ulamulilo wamphamvu padziko lonse wa Britain na America uzilephela kucita zinthu mwamphamvu mmene ungathele.

  • Chati yaciŵili pa machati 4, yoonetsa maulosi osiyana-siyana ofotokoza za masiku otsiliza ano. Maulosiwa afotokoza zocitika kuyambila m’caka ca 1919 mpaka 1945, ndipo zina mwa zocitikazo zinacitika pa nthawi imodzi. Boma la Germany ndilo linali mfumu ya kumpoto mpaka kudzafika mu 1945. Ulamulilo wa Mphamvu Padziko Lonse wa Britain na America ndiwo unakhala mfumu ya kum’mwela. Ulosi 6: Mu 1919, Akhristu odzozedwa anayamba kusonkhanitsidwa mumpingo wobwezeletsedwa. Kuyambila mu 1919, nchito yolalikila yapitilizabe ndipo ikupita patsogolo. Ulosi 7: Mu 1920, bungwe la League of Nations linakhazikitsidwa, ndipo linagwila nchito mpaka kuciyambi kwa Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse. Chati ionetsanso izi: Ulosi 1, cilombo ca mitu 7 cikalipo. Ulosi 5, mapazi acitsulo cosakanizika na dongo akalipo. Zocitika padzikoli kuyambila mu 1939 mpaka 1945, Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse. Zocitika zokhudza anthu a Yehova: Kuyambila mu 1933 mpaka mu 1945, Mboni za Yehova zoposa 11,000 zinaponyedwa m’ndende ku Germany. Kuyambila mu 1939 mpaka mu 1945, Mboni pafupi-fupi 1,600 zinaponyedwa m’ndende ku Britain. Kuyambila mu 1940 mpaka mu 1944, Mboni zinacitidwa cipongwe na magulu aciwawa nthawi zoposa 2,500.
    Ulosi 6.

    (Ma)lemba Mat. 13:30; 24:14, 45; 28:19, 20

    Ulosi “Tiligu” akumusonkhanitsa na kumuika “m’nkhokwe,” ndipo “kapolo wokhulupilika ndi wanzelu” anaikidwa kuti aziyang’anila anchito apakhomo. “Uthenga wabwino uwu wa ufumu” unayamba kulalikidwa “padziko lonse lapansi kumene kuli anthu.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mu 1919, kapolo wokhulupilika anaikidwa kuti aziyang’anila anthu a Mulungu. Kuyambila pa nthawiyo, Ophunzila Baibo anawonjezela cangu cawo pa nchito yolalikila. Masiku ano, Mboni za Yehova zimalalikila m’maiko oposa 200, ndiponso zimafalitsa mabuku ophunzilila Baibo m’vitundu voposa 1,000.

  •  Ulosi 7.

    (Ma)lemba Dan. 12:11; Chiv. 13:11, 14, 15

    Ulosi Cilombo ca nyanga ziŵili cinauza anthu “kupanga cifanizilo ca cilombo” ca mitu 7 komanso cinapeleka ‘mpweya ku cifaniziloco.’

    Kukwanilitsidwa kwake Ulamulilo wamphamvu padziko lonse wa Britain na America unayambitsa bungwe la League of Nations. Maiko enanso anayamba kucilikiza bungweli. M’kupita kwa nthawi, mfumu ya kumpoto nayonso inaloŵa m’bungweli. Koma inangokhalamo kuyambila mu 1926 mpaka mu 1933. Anthu anali kukhulupilila kuti bungwe la League of Nations lidzabweletsa mtendele padziko lonse, pamene m’ceni-ceni ni Ufumu wa Mulungu wokha ungacite zimenezi. Masiku ano, anthu amakhulupililanso kuti United Nations idzabweletsa mtendele padziko lonse.

  • Chati yacitatu pa machati 4, yoonetsa maulosi osiyana-siyana ofotokoza za masiku otsiliza ano. Maulosiwa afotokoza zocitika kuyambila m’caka ca 1945 mpaka 1991, ndipo zina mwa zocitikazo zinacitika pa nthawi imodzi. Boma la Soviet Union na maiko ogwilizana nalo ndiwo anali mfumu ya kumpoto mpaka mu 1991. Pambuyo pake Russia na maiko ogwilizana naye ndiwo anakhala mfumu ya kumpoto. Ulamulilo Wamphamvu Padziko Lonse wa Britain na America ndiwo unali Mfumu ya kum’mwela. Ulosi 8: Ciusi ca bomba la nyukiliya, comwe cionetsa kuti Ulamulilo Mphamvu Padziko Lonse wa Britain na America wapha anthu ambili na kuwononga zinthu zambili. Ulosi 9: Bungwe la United Nations linakhazikitsa mu 1945, kulowa m’malo bungwe la League of Nations. Chati ionetsanso izi: Ulosi 1, cilombo ca mitu 7 cokalipo. Ulosi 5, mapazi acitsulo cosakanizika na dongo akalipo. Ulosi 6, mu 1945, panali ofalitsa oposa 156,000. Mu 1991, panali ofalitsa oposa 4,278,000. Zocitika zokhudza anthu a Yehova: Kuyambila mu 1945 mpaka m’zaka za m’ma 1950, boma la Soviet Union linathamangitsila ku Siberia Mboni masausande ambili.
    Ulosi 8.

    Lemba Dan. 8:​23, 24

    Ulosi Mfumu ya maonekedwe oopsa “idzawononga zinthu zambili.”

    Kukwanilitsidwa kwake Ulamulilo Wamphamvu Padziko Lonse wa Britain na America unapha anthu ambili komanso unawononga zinthu zambili. Mwacitsanzo, pa Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse, dziko la America linaponya mabomba aŵili a nyukiliya m’dziko lodana na Britain na America. Mabombawo anapha anthu ambili komanso anawononga zinthu zoculuka kuposa cida cina ciliconse.

  • Ulosi 9.

    (Ma)lemba Dan. 11:31; Chiv. 17:​3, 7-11

    Ulosi ‘Cilombo cofiila kwambili’ cokhala na nyanga 10 cinatuluka m’phompho, ndipo ndico mfumu ya 8. Buku la Danieli limachula mfumu imeneyi kuti “cinthu conyansa cobweletsa ciwonongeko.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mkati mwa Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse Bungwe la League of Nations linaleka kugwila nchito. Nkhondoyo itatha, bungwe la United Nations ‘linaikidwa pamalowo,’ kapena kuti linakhazikitsidwa. Mofanana na League of Nations, bungwe la United Nations limapatsidwa ulemelelo woyenela kupelekedwa ku Ufumu wa Mulungu. Bungweli lidzaukila zipembedzo zonama.

  •  Chati yothela pa machati 4, yoonetsa maulosi osiyana-siyana ofotokoza za masiku otsiliza. Maulosiwa afotokoza zocitika za masiku ano mpaka kukadutsa nkhondo Aramagedo. Russia na maiko ogwilizana naye ndiwo mfumu ya kumpoto. Ulamulilo Wamphamvu Padziko Lonse wa Britain na America ndiwo mfumu ya kum’mwela. Ulosi 10: Atsogoleli a maiko adzalengeza ‘bata ndi mtendele.’ Kenako, cisautso cacikulu cidzayamba. Ulosi 11: Maboma adzaukila zipembedzo zonama. Ulosi 12: Maboma a dziko adzaukila anthu a Mulungu. Otsalila odzozedwa adzasonkhanitsidwa kupita kumwamba. Ulosi 13: Aramagedo. Wokwela pa hosi yoyela adzatsiliza kugonjetsa adani ake. Cilombo ca mitu 7 cidzawonongedwa; mapazi acitsulo cosakanizika na dongo acifanizilo cacikulu adzapwanyidwa. Chati ionetsanso izi: Ulosi 1, cilombo ca mitu 7 cidzakhalapobe mpaka pa Aramagedo. Ulosi 5, mapazi acitsulo cosakanizika na dongo adzapitiliza adzakhalapobe mpaka pa Aramagedo. Ulosi 6, tsopano pali ofalitsa oposa 8,580,000. Zocitika zokhudza anthu a Yehova: Mu 2017, boma la Russia linaponya m’ndende Mboni na kulanda ofesi yanthambi.
    Ulosi wa 10 komanso wa 11.

    (Ma)lemba 1 Ates. 5:3; Chiv. 17:16

    Ulosi Atsogoleli a maiko adzalengeza “Bata ndi mtendele!” Kenako “nyanga 10” komanso “cilombo,” zidzaukila “hulelo” na kuliwononga. Pambuyo pake, mitundu ya anthu idzawonongedwa.

    Kukwanilitsidwa kwake Atsogoleli a maiko adzalengeza kuti akwanitsa kubweletsa bata na mtendele padzikoli. Ndiyeno, maiko amene amacilikiza bungwe la United Nations adzawononga zipembedzo zonama. Ici cidzakhala ciyambi ca cisautso cacikulu. Cisautso cacikulu cidzatha pamene Yesu adzawononga mbali yotsala ya dziko la Satana pa Aramagedo.

  • Ulosi 12.

    (Ma)lemba Ezek. 38:11, 14-17; Mat. 24:31

    Ulosi Gogi adzaukila dziko la anthu a Mulungu. Ndiyeno, angelo adzasonkhanitsa anthu “osankhidwa.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mfumu ya kumpoto pamodzi na maboma ena onse adzaukila anthu a Mulungu. Panthawi inayake kuukilako kuli mkati, otsalila odzozedwa adzatengedwa kupita kumwamba.

  • Ulosi 13.

    (Ma)lemba Ezek. 38:18-23; Dan. 2:34, 35, 44, 45; Chiv. 6:2; 16:14, 16; 17:14; 19:20

    Ulosi ‘Wokwela’ pa “hachi yoyela” adzatsiliza ‘kugonjetsa adani ake’ mwa kuwononga Gogi na gulu lake la nkhondo. “Cilombo” ‘cidzaponyedwa m’nyanja ya moto,’ komanso cifanizilo cacikulu cidzaphwanyidwa-phwanyidwa.

    Kukwanilitsidwa kwake Yesu, Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, adzabwela kudzapulumutsa anthu a Mulungu. Iye pamodzi na olamulila anzake 144,000, komanso magulu ankhondo a angelo, adzawononga mitundu yonse ya anthu oukila anthu a Mulungu. Uku ndiye kudzakhala kutha kwa dziko la Satana.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani