LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp25 na. 1 tsa. 3
  • Pa Nkhondo Pamacitika Zinthu Zoipa Kwambili

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Pa Nkhondo Pamacitika Zinthu Zoipa Kwambili
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • ZIMENE ASILIKALI ANAKAMBA
  • ZIMENE ANTHU ENA ANAKAMBA
  • Kupeza Mtendele wa Mumtima pa Nthawi ya Nkhondo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Nkhondo ya ku Ukraine IIoŵa Caka Caciŵili—Kodi Baibo Ipeleka Ciyembekezo Cotani?
    Nkhani Zina
  • Ndalama Matililiyoni Zawonongedwa pa Nkhondo—Koma Kodi ni Ndalama Zokha Zawonongeka?
    Nkhani Zina
  • Mmene Nkhondo Zimatikhudzila Tonsefe
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
wp25 na. 1 tsa. 3
Zithunzi: 1. Cithunzi cong’ambika coonetsa gawo lapamwamba la nkhope ya msilikali. 2. Cithunzi cong’ambika coonetsa gawo lapamwamba la nkhope ya mzimayi wokalamba.

Pa Nkhondo Pamacitika Zinthu Zoipa Kwambili

Nkhondo ndi cimodzi mwa zinthu zimene zimabweletsa mavuto aakulu kwa anthu. Asilikali komanso anthu amene anakhalako kumalo kumene kunali nkhondo amawadziwa bwino mavuto amenewa.

ZIMENE ASILIKALI ANAKAMBA

“Nthawi zonse umaona anthu akuphedwa kapena kuvulazidwa koopsa. Nthawi zonse umaona kuti ndiwe wosatetezeka.”​—Gary, wa ku Britain.

“Ndinaombeledwa kumsana ndi kumaso, ndipo n’nali kuona anthu ambili akuphedwa, kuphatikizapo ana komanso okalamba. Nkhondo imakupangitsa kukhala wouma mtima.”​—Wilmar, wa ku Colombia.

“Munthu wina akaombeledwa ukuona, sumaiwala zocitikazo. Nthawi zonse m’maganizo umakhala ukumuona komanso kumumva akulila. Sumamuiwala munthuyo ngakhale pang’ono.”​—Zafirah, wa ku United States.

ZIMENE ANTHU ENA ANAKAMBA

“N’nali kuona kuti n’zosatheka kukhalanso wacimwemwe. Umakhala ndi nkhawa yakuti udzaphedwa. Koma umakhalanso ndi nkhawa yaikulu yakuti a m’banja lako komanso anzako adzaphedwa.”​—Oleksandra, wa ku Ukraine.

“Tinali kukhala ndi mantha tikaimilila pa mzele wolandila cakudya kucokela ca m’ma 02:00 kukafika ca m’ma 23:​00, cifukwa tinali kudziwa kuti nthawi ina iliyonse tikhoza kuombeledwa.”​—Daler, wa ku Tajikistan.

“Makolo anga anaphedwa pa nkhondo. N’nakhala wamasiye, ndipo n’nalibe aliyense wonditonthoza kapena wondisamalila.”​—Marie, wa ku Rwanda.

Ngakhale kuti anthuwa anakumana ndi mavuto cifukwa ca nkhondo, iwo tsopano ali ndi mtendele wa mumtima. Ndipo ndi otsimikiza kuti nkhondo zonse zidzatha posacedwa. Magazini ino ya Nsanja ya Mlonda idzagwilitsa nchito Baibo pofotokoza mmene zimenezi zidzacitikila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani