LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 October tsa. 32
  • Zimene Mungacite Kuti Muziwelenga Baibo Tsiku Lililonse

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Zimene Mungacite Kuti Muziwelenga Baibo Tsiku Lililonse
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • Mmene Tingagwilitsile Nchito Zinthu Zongomvetsela za pa jw.org
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Kodi Mumaigwilitsa Nchito Mofikapo Baibo Yongomvetsela?
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Zimene Mungacite Kuti Muzipindula Kwambili Poŵelenga Baibo
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Tingacite Ciani Kuti Tikulitse Cikondi Cathu kwa Mulungu na kwa Mnansi Wathu?
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 October tsa. 32

MFUNDO YOTHANDIZA PA KUWELENGA KWANU

Zimene Mungacite Kuti Muziwelenga Baibo Tsiku Lililonse

Pokhala ndi zocita zambili, kodi nthawi zina zimakubvutani kutsatila pulogilamu yanu yowelenga Mau a Mulungu tsiku lililonse? (Yos. 1:8) Ngati n’conco, yesani malingalilo otsatilawa:

  • Chelani alamu. Chelani alamu pa cipangizo kuti izikukumbutsani kuti muwelenge Baibo.

  • Ikani Baibo pa malo oonekela bwino. Ngati mumawelenga Baibo yopulinta, muziiika pa malo oonekela kuti muziiona mosabvuta tsiku lililonse.​—Deut. 11:18.

  • Muzimvetsela Baibo ya mau. Muzimvetsela Baibo ya mau pomwe mukugwila nchito za tsiku ndi tsiku. Pa nkhaniyi, mpainiya wina dzina lake Tara, amenenso ndi mai ndipo amagwila nchito usiku, anakamba kuti: “Ndikamamvetsela Baibo ya mau pomwe ndikugwila nchito za pakhomo, zimakhala kuti ndikuwelenga Baibo.”

  • Limbikilani. Ngati zocitika zosayembekezeleka zasokoneza pulogilamu yanu, mungawelengeko mavesi ocepa musanagone. Ngakhale mutamawelenga kambali kocepa tsiku lililonse, mudzapindulabe kwambili.​—1 Pet. 2:2.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani