Mfundo ya Kumapeto
^ [1] (palagilafu 14) Pali zolinganako zambili pakati pa ukapolo wa Ayuda wa zaka 70 ku Babulo, na zimene zinacitika kwa Akhiristu mpatuko utayamba. Komabe, sizikuoneka kuti ukapolo wa Ayuda kweni-kweni unacitila cithunzi zimene zinali kudzacitika kwa Akhiristu. Mwacitsanzo, utali wa zaka za ukopolo unali wosiyana. Conco, sitiyenela kuyesa kugwilizanitsa mbali zonse-zonse za ukapolo wa Ayuda ndi zimene zinacitika kwa Akhiristu odzozedwa m’zaka zokafikitsa ku 1919.