Mawu Amunsi
a Ponena za angelo olungama, lemba la Chivumbulutso 5:11 limakamba kuti: “Ciŵelengelo cao cinali miyanda kuculukitsa ndi miyanda ndiponso masauzande kuculukitsa ndi masauzande,” kapena kuti “10,000 kuculukitsa ndi ma 10,000.” (Mau apansi) Conco, Baibo imaonetsa kuti Mulungu analenga angelo mamiliyoni ambili-mbili.