Mawu Amunsi
a M’malemba Aciheberi mulibe liu lenileni lotanthauza “cikumbumtima.” Komabe mogwilizana ndi citsanzo ici, pali umboni woonekelatu wakuti anthu anali kumvela cikumbumtima cao. Liu lakuti “mtima” nthawi zambili limatanthauza munthu wamkati. Koma pa lembali, liu limeneli limakamba za cikumbumtima, cimene ndi mbali imodzi cabe ya munthu wamkati. Liu la Cigiriki lotembenuzidwa kuti “cikumbumtima” limaonekela nthawi 30 m’Malemba Acigiriki Acikristu.