Mawu Amunsi
a Kodi timadziŵa bwanji kuti Atate anaphunzitsa Mwana wake mmene angaphunzitsile ena? Ganizilani izi: Yesu anali kukonda kugwilitsila nchito mafanizo polalikila, ndipo zimenezi zinakwanilitsa ulosi umene unalembedwa zaka zambilimbili iye asanabadwe. (Sal. 78:2; Mat. 13:34, 35) Mwacionekele, Mlembi wamkulu wa ulosiwo, Yehova, anadziŵilatu kuti Mwana wake adzagwilitsila nchito mafanizo pophunzitsa.—2 Tim. 3:16, 17.