Mawu Amunsi
e Ndime 14: Kumeneku ndi kusintha kwa kamvedwe kathu ka lemba la Mateyu 13:42. M’mbuyomu, zofalitsa zathu zinali kufotokoza kuti Akristu onama akhala akulila ndi kukukuta mano kwa zaka zambili cifukwa cakuti, “ana a ufumu” akhala akuwavumbula kuti io ndi “ana a woipayo.” (Mat. 13:38) Komabe, zimene tiyenela kudziŵa ndi zakuti, kukukuta mano kumeneku ndi kogwilizana ndi cionongeko.—Sal. 112:10.