Mawu Amunsi
f Ndime 16: Lemba la Danieli 12:3 limakamba kuti “Anthu ozindikila [Akristu odzozedwa] adzawala ngati kuwala kwa kuthambo.” Akali padziko lapansi, io amacita zimenezi mwa kutengako mbali mu nchito yolalikila. Koma Mateyu 13:43 imakamba za nthawi pamene io adzawala kwambili mu Ufumu wakumwamba. Poyamba, tinali kukhulupilila kuti malemba onse aŵili amenewa amanena za nchito yolalikila.