Mawu Amunsi
b Mulungu amadana ndi anthu amene amalekana pa zifukwa zosayenela. Koma ngati wina m’cikwati wacita dama, Mulungu amapatsa munthu wosalakwayo ufulu wothetsa cikwati kapena ai. (Malaki 2:16; Mateyu 19:9) Onani nkhani yakuti “Lingalilo la Baibulo—Kodi Nkusudzula kwa Mtundu Wotani Kumene Mulungu Amada?” mu Galamukani! ya February 8, 1994 yofalitsidwa ndi Mboni za Yehova.