Mawu Amunsi
a Buku lakuti Insight on the Scriptures, voliyamu 2 tsamba 247, limakamba kuti asayansi poyesa kufotokoza zimene zimacititsa kuti tizikalamba ndi kufa, amaiŵala mfundo imodzi yofunika. Iwo amalephela kuzindikila kuti Mlengi ndiye anaweluza anthu oyamba kuti azifa. Ndiye cifukwa cake samvetsetsa cimene cimacititsa kuti tizikalamba ndi kufa.